< 1 Samuel 3 >

1 Now, the boy Samuel, was ministering unto Yahweh, before Eli, —and, the word of Yahweh, had become rare in those days, there was no well-known vision.
Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.
2 But it came to pass, at that time, when Eli was lying down in his place, his eyes, having begun to be dim, he could not see,
Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake.
3 though, the lamp of God, was not yet to be put out, and, Samuel, was lying down in the temple of Yahweh, where was the ark of God,
Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
4 that Yahweh called unto Samuel, and he said—Behold me!
Yehova anayitana Samueli. Iye anayankha kuti, “Wawa.”
5 So he ran unto Eli and said—Behold me! for thou calledst me. And he said—I called not, return—Its down. So he went, and lie down.
Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.” Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.
6 And again Yahweh called once there—Samuel! Then rose Samuel, and went unto Eli, and said—Behold me! for thou calledst me. And he said—I called not, my son, return—lie down.
Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.” Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”
7 Now, Samuel, as yet knew not Yahweh, —nor, as yet, had been revealed unto him, the word of Yahweh.
Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.
8 And again Yahweh called—Samuel! a third time. Then he arose, and went unto Eli, and said—Behold me! for thou calledst me. Then did Eli perceive, that, Yahweh, was calling the boy.
Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.” Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo.
9 So Eli said to Samuel—Go, lie down, and it shall be, if he call unto thee, that thou shalt say—Speak, Yahweh, for thy servant is listening. And Samuel went, and lay down in his place.
Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.
10 Then came Yahweh, and stood, and called as time after time—Samuel! Samuel! And Samuel said, Speak, for thy servant is listening.
Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!” Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”
11 And Yahweh said unto Samuel, Lo! I am doing a thing, in Israel, —at which both ears of everyone that heareth it shall tingle.
Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve.
12 In that day, will I confirm against Eli, all that I have spoken against his house, —beginning and finishing.
Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza.
13 Therefore do I tell him, that I am about to judge his house unto times age-abiding, for the iniquity which he knoweth, in that his sons are cursing God, and he hath not rebuked them.
Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa.
14 And therefore have I sworn, respecting the house of Eli, —that the iniquity of the house of Eli shall receive no propitiatory-covering, by sacrifice or by present, unto times age-abiding.
Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’”
15 And Samuel lay until the morning, and rose early in the morning, and opened the doors of the house of Yahweh, —but, Samuel, feared to tell the appearing, unto Eli.
Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake.
16 So Eli called Samuel, and said—Samuel! my son. And he said—Behold me!
Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.” Samueli anayankha kuti, “Wawa.”
17 And he said—What is the word, which he spake unto thee? I pray thee, do not hide it from me. So, let God do to thee, and, so, let him add, if thou hide from me a word, out of anything which he hath spoken unto thee.
Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.”
18 So Samuel told him all the words, and hid nothing from him. And he said, Yahweh, he is; what is good in his own eyes, let him do.
Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”
19 And Samuel grew, —and, Yahweh, proved to he with him, and let none of all his words fall to the ground.
Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi.
20 So all Israel, from Dan even to Beersheba, came to know, —that Samuel had become confirmed as a prophet unto Yahweh.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake.
21 Thus did Yahweh again appear in Shiloh, —for Yahweh had revealed himself unto Samuel in Shiloh, in the word of Yahweh.
Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.

< 1 Samuel 3 >