< 1 Kings 12 >

1 And Rehoboam went to Shechem, —for, to Shechem, had all Israel come to make him king.
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse nʼkuti atapita kumeneko kukamulonga ufumu.
2 And it came to pass, when Jeroboam son of Nebat heard of it—he being yet in Egypt, whither he had fled from the face of Solomon the king, that Jeroboam returned from Egypt;
Yeroboamu mwana wa Nebati anamva zimenezi. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamuyo akukhala ku Igupto, pakuti atathawa Mfumu Solomoni iyeyo anakakhala ku Igupto.
3 yes they sent, and called him, and Jeroboam and all the convocation of Israel came, —and spake unto Rehoboam, saying:
Tsono anthu anayitanitsa Yeroboamu, ndipo iye pamodzi ndi gulu lonse la ku Israeli anapita kwa Rehobowamu ndipo anamuwuza kuti,
4 Thy father, made our yoke, grievous, —now, therefore do, thou, lighten the grievous service of thy father, and his heavy yoke which he put upon us, that we may serve thee.
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa kwambiri, koma inu chepetsani ntchito yowawa pa ife ndipo peputsani goli lolemetsa limene anatisenzetsa. Mukatero tidzakutumikirani.”
5 And he said unto them—Depart ye for yet three days, and then come again unto me. And the people departed.
Rehobowamu anayankha kuti, “Pitani, ndipo pakatha masiku atatu, mudzabwerenso.” Choncho anthuwo anapitadi.
6 Then King Rehoboam consulted the elders who used to stand before Solomon his father, while he yet lived, saying, —How do, ye, advise, that I answer this people?
Ndipo Mfumu Rehobowamu anapempha nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira Solomoni abambo ake pamene anali ndi moyo. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu amenewa?”
7 And they spake unto him, saying—If, to-day, thou wilt be servant unto this people, and wilt serve them, —and answer them kindly, and speak unto them good words, then will they be, thy, servants, always.
Iwo anayankha kuti, “Ngati lero mudzakhala mtumiki wa anthu amenewa ndi kuwatumikira ndipo mukawayankha bwino, iwowo adzakhala atumiki anu nthawi zonse.”
8 But he declined the counsel of the elders which they gave him, and consulted with the young men, who had grown up with him, who were standing before himself;
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakuluwo anamupatsa ndipo anafunsira nzeru kwa anyamata anzake amene anakulira nawo limodzi omwe ankamutumikira.
9 and said unto them—What counsel do, ye, give as to how we shall answer this people who have spoken unto me, saying—Make a lightening of the yoke which thy father put upon us?
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ngotani? Kodi ndiwayankhe chiyani anthu amene akunena kwa ine kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anatisenzetsa’?”
10 Then spake unto him the young men who had grown up with him, saying, Thus, shalt thou say to this people that have spoken unto thee, saying—Thy father, made our yoke heavy, thou, therefore lighten it upon us, Thus, shalt thou speak unto them, My little finger, is thicker than my father’s loins;
Anyamata anzake amene anakula nawo limodzi aja anamuyankha kuti, “Anthu amene ananena kwa iwe kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa, koma inu peputsani goli lathu,’ uwawuze kuti ‘Chala changa chakanise nʼchachikulu kupambana chiwuno cha abambo anga.
11 Now, therefore, whereas, my father, laid upon you a heavy yoke, I, will add to your yoke, —My father, did chastise you with whips, but, I, will chastise you with scorpions.
Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 So Jeroboam and all the people came in unto Rehoboam, on the third day, —as the king had bidden, saying—Come again unto me, on the third day.
Patapita masiku atatu, Yeroboamu pamodzi ndi anthu onse anabwera kwa Rehobowamu, monga momwe inanenera mfumu kuti, “Mudzabwere pakatha masiku atatu.”
13 And the king answered the people, harshly, —and declined the counsel of the elders wherewith they had counselled him;
Mfumuyo inawayankha anthuwo mwankhanza. Kukana malangizo amene akuluakulu anayipatsa.
14 and spake unto them after the counsel of the young men, saying, My father, made your yoke heavy, but, I, will add unto your yoke, —My father, chastised you, with whips, but, I, will chastise you, with scorpions.
Anatsatira malangizo amene anyamata anzake anamupatsa ndipo anati “Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa. Ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 Thus the king hearkened not unto the people, —for there had come about a turn from Yahweh, that he might establish his word, which Yahweh had spoken by Ahijah the Shilonite, unto Jeroboam, son of Nebat.
Choncho mfumu sinamvere pempho la anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Yehova, kukwaniritsa mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 So when all Israel saw that the king hearkened not unto them, the people answered the king, saying—What portion have, we, in, David. Or inheritance in the son of Jesse? To your homes O Israel! Now, see to thine own house, O David! And Israel departed to their homes.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kumva zopempha zawo, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, ndi gawo lanjinso mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli, bwererani ku matenti anu! Ziyangʼanira nyumba yako, Iwe Davide!” Kotero Aisraeli anachoka napita ku nyumba zawo.
17 But, as for the sons of Israel who were dwelling in the cities of Judah, Rehoboam reigned over them.
Koma Aisraeli amene ankakhala mʼmizinda ya Yuda ankalamuliridwa ndi Rehobowamu.
18 Then King Rehoboam sent Adoniram who was over the tribute, but all Israel stoned him with stones, that he died, —King Rehoboam, therefore, hastily mounted his chariot, to flee unto Jerusalem.
Mfumu Rehobowamu anatuma Adoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli onse anamugeda ndi miyala mpaka kumupha. Koma Mfumu Rehobowamu anakwera msangamsanga galeta wake nathawira ku Yerusalemu.
19 So Israel rebelled against the house of David, —unto this day.
Choncho Aisraeli akhala akuwukira nyumba ya Davide mpaka lero lino.
20 And it came to pass, when all Israel heard that Jeroboam had returned, that they sent and called him into the assembly, and made him king over all Israel, —there were none that followed the house of David, saving the tribe of Judah only.
Aisraeli onse atamva kuti Yeroboamu wabwerera kuchokera ku Igupto, anatumiza mawu okamuyitana kuti abwere ku msonkhano ndipo anamuyika kukhala mfumu ya Aisraeli onse. Fuko la Yuda lokha ndi lomwe linkatsatira nyumba ya Davide.
21 And, when Rehoboam entered Jerusalem, he called together all the house of Judah and the tribe of Benjamin—a hundred and eighty thousand chosen men, able to make war, —to fight against the house of Israel, to bring back the kingdom to Rehoboam, son of Solomon.
Rehobowamu atafika ku Yerusalemu, anasonkhanitsa nyumba yonse ya Yuda ndi fuko la Benjamini, nasankha ankhondo okwanira 180,000, kuti akamenyane ndi nyumba ya Israeli kuti amubwezere Rehobowamu mwana wa Solomoni ufumu wake.
22 Then came the word of God unto Shemaiah, the man of God, saying:
Koma Mulungu anayankhula ndi Semaya, munthu wa Mulungu kuti,
23 Speak unto Rehoboam, son of Solomon, king of Judah, and unto all the house of Judah, and Benjamin, —and the remnant of the people, saying:
“Nena kwa Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda, kwa nyumba yonse ya Yuda ndi Benjamini, ndiponso kwa anthu ena onse kuti,
24 Thus, saith Yahweh—Ye shall not go up, neither shall ye fight with your brethren the sons of Israel, —return ye every man to his own house, for, from me, hath this thing been brought about. So they hearkened unto the word of Yahweh, and turned back to depart, according to the word of Yahweh.
‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu Aisraeli. Aliyense wa inu abwerere kwawo, pakuti zimenezi ndachita ndine.’” Choncho anthuwo anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera kwawo, monga analamulira Yehova.
25 Then Jeroboam built Shechem, in the hill country of Ephraim, and dwelt therein, —and went forth from thence, and built Penuel.
Tsono Yeroboamu anamanga mzinda wa Sekemu mʼdziko la mapiri la Efereimu ndipo anakhala kumeneko. Kuchokera kumeneko anapita kukamanga mzinda wa Penueli.
26 And Jeroboam said in his heart, —Now, shall the kingdom return to the house of David:
Yeroboamu anaganiza mu mtima mwake kuti, “Ndithu, ufumuwu udzabwereranso ku nyumba ya Davide.
27 If this people go up to offer sacrifices in the house of Yahweh, in Jerusalem, then will the heart of this people return unto their lord, unto Rehoboam, king of Judah, —and they will slay me, and return unto Rehoboam, king of Judah.
Ngati anthuwa azipitabe kukapereka nsembe ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu, adzayambanso kutsatira mbuye wawo Rehobowamu, mfumu ya Yuda. Adzandipha ndi kubwerera kwa Mfumu Rehobowamu.”
28 Whereupon the king took counsel, and made two calves of gold, —and said unto them—It is, too much for you, to go up to Jerusalem, Lo! thy gods, O Israel, that brought thee up out of the land of Egypt;
Itapempha nzeru, mfumuyo inapanga mafano awiri a ana angʼombe. Mfumuyo inati kwa anthuwo, “Mwakhala mukupita ku Yerusalemu nthawi yayitali. Iwe Israeli, nayi milungu yako imene inakutulutsa mʼdziko la Igupto.”
29 And he set the one in Bethel, —and, the other, put he in Dan.
Fano lina analiyika ku Beteli ndipo lina analiyika ku Dani.
30 And this thing became a sin, —and the people went before the one, as far as Dan.
Ndipo zimenezi zinachimwitsa anthu pakuti anthu ankapita mpaka ku Dani kukapembedza fano limene linali kumeneko.
31 And he made a house of high-places, —and made priests from the whole compass of the people, who were not of the sons of Levi.
Yeroboamu anamanga Nyumba za Mulungu pa malo azipembedzo nasankha ansembe kuchokera pakati pa anthu wamba, ngakhale sanali Alevi.
32 And Jeroboam made a festival in the eight month, on the fifteenth day of the month, like the festival which [was held] in Judah, and offered up on the altar, likewise, did he in Bethel, sacrificing to the calves which he had made, —and he kept in attendance in Bethel, the priests of the high-places which he had made.
Iye anakhazikitsa chikondwerero pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, lofanana ndi tsiku la chikondwerero cha ku Yuda, ndipo ankapereka nsembe pa guwa. Izi ankachita ku Beteli, kupereka nsembe kwa ana angʼombe amene anapanga. Ndipo ku Beteliko anayikako ansembe pa malo achipembedzo amene anamanga.
33 And he offered up on the altar which he had made in Bethel, on the fifteenth day in the eighth month, in the month which he had devised out of his own heart, —thus made he a festival for the sons of Israel, and offered up on the altar, to make a perfume.
Tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, mwezi umene anawusankha yekha, anapereka nsembe pa guwa limene analimanga ku Beteli. Motero anakhazikitsa chikondwerero cha Aisraeli ndipo iye ankapita kukapereka nsembe yofukiza lubani pa guwa.

< 1 Kings 12 >