< 1 Kings 1 >

1 Now, King David, was old, advanced in days, —and they covered him with clothes, but he gat no heat.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Wherefore his servants said unto him—Let there be sought for my lord the king, a young woman—a virgin, so shall she stand before the king, that she may become his companion, —and she shall lie in thy bosom, and my lord the king shall get, heat.
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 So they sought a fair young woman, throughout all the bounds of Israel, —and found Abishag, the Shunammite, and brought her in, unto the king.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Now, the young woman, was exceeding fair, —so she became unto the king a companion, and ministered unto him, but, the king, knew her not.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 And, Adonijah son of Haggith, exalted himself, saying—I, will be king. Therefore prepared he for himself chariots and horsemen, and fifty men to run before him.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 Now his father had not displeased him all his days, by saying—Why, thus, hast thou done? Moreover also, he, was of exceeding handsome appearance, and, him, did his mother bear, after Absolom.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 So then he had speech with Joab, son of Zeruiah, and with Abiathar the priest, —and they gave help, following Adonijah.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 But, Zadok the priest, and Benaiah son of Jehoiada, and Nathan the prophet, and Shimei, and Rei, and the mighty men who belonged to David, were not with Adonijah.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 And Adonijah sacrificed sheep and oxen and heifers, near the stone of Zoheleth, which is beside En-rogel, —and invited all his brethren, sons of the king, and all the men of Judah, servants of the king;
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 but, Nathan the prophet, and Benaiah, and the mighty men, and Solomon his brother, he invited not.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Then spake Nathan unto Bath-sheba mother of Solomon, saying—Hast thou not heard that Adonijah son of Haggith hath become king, and, our lord David, knoweth it not?
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Now, therefore, come; let me give thee counsel, I pray thee, —so shalt thou rescue thine own life, and the life of thy son, Solomon.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Go, and get thee in unto King David, and thou shalt say unto him—Didst not, thou thyself, my lord O king, swear unto thy handmaid, saying—Solomon thy son, shall become king after me, yea, he, shall sit upon my throne? Why, then, hath, Adonijah, become king?
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Lo! while thou art yet speaking there with the king, I also, will come in after thee, and confirm thy words.
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 So Bath-sheba went in unto the king, into the chamber, now, the king, was very old, —and Abishag the Shunammite, was ministering unto the king.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 And Bath-sheba bowed, and did homage unto the king, —and the king said—What aileth thee?
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 And she said unto him—My lord, thou thyself, didst swear by Yahweh thy God, unto thy handmaid, Assuredly, Solomon thy son, shall become king after me, —yea, he, shall sit upon my throne.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 But, now, lo! Adonijah, hath become king; now, therefore, my lord, O king, thou knowest it not:
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 and he hath sacrificed oxen and heifers and sheep, in abundance, and hath invited all the sons of the king, and Abiathar the priest, and Joab general of the army, —but, Solomon thy servant, hath he not invited.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Thou, therefore, my lord, O king, the eyes of all Israel, are upon thee, —to tell them, who shall sit upon the throne of my lord the king, after him.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 Otherwise it shall come to pass, when my lord the king shall sleep with his fathers, then shall I and my son Solomon be counted, offenders.
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 And lo! while yet she was speaking with the king, Nathan the prophet, came in.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 So they told the king, saying, Lo! Nathan the prophet! And, when he had come in before the king, he bowed himself down to the king with his face to the ground.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Then said Nathan—My lord, O king, hast, thou, said, Adonijah, shall become king after me, —yea, he, shall sit upon my throne?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 For he hath gone down to-day, and hath sacrificed oxen and heifers and sheep, in abundance, and hath invited all the sons of the king, and the generals of the army, and Abiathar the priest, and, there they are—eating and drinking before him, —and they have said—Long live King Adonijah!
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 But, me, even me thy servant, and Zadok the priest, and Benaiah son of Jehoiada, and Solomon thy servant, hath he not invited.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 If, of my lord the king, this thing had been brought to pass, then wouldest thou not have made known unto thy servant, who should sit upon the throne of my lord the king, after him?
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Then responded King David, and said, Call me Bath-sheba. So she came in before the king, and stood before the king.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 And the king sware, and said, —By the life of Yahweh, who hath redeemed my life out of every strait,
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 even as I sware unto thee by Yahweh, God of Israel, saying, Assuredly, Solomon thy son, shall become king after me, yea, he, shall sit upon my throne, in my stead, even so, will I do this day.
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 Then Bath-sheba bowed with her face to the ground, and did homage unto the king, —and said—Let my lord, King David, live to times age-abiding!
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Then said King David—Call me Zadok the priest, and Nathan the prophet, and Benaiah son of Jehoiada. And they came in before the king.
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 Then said the king unto them—Take ye with you the servants of your lord, and cause Solomon my son to ride upon the mule which pertaineth unto myself, —and bring him down unto Gihon;
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 then shall Zadok the priest and Nathan the prophet anoint him there as king over Israel, —and ye shall blow with the horn, and say—Long live King Solomon!
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Then shall ye come up after him, and he shall enter, and sit upon my throne, yea, he, shall become king in my stead; even, him, have I charged to become leader, over Israel, and over Judah.
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 Then did Benaiah son of Jehoiada make response unto the king, and say—Amen! so, say Yahweh, God of my lord the king.
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 As Yahweh hath been with my lord the king, so, let him he with Solomon, —and make his throne greater than the throne of my lord, King David.
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 So Zadok the priest, and Nathan the prophet, and Benaiah son of Jehoiada, with the Cherethites and the Pelethites, went down, and caused Solomon to ride upon the mule of King David, —and they escorted him to Gihon.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 Then took Zadok the priest, the horn of oil out of the Tent, and anointed Solomon, —and they blew with a [ram’s] horn, and all the people said, Long live King Solomon!
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 And all the people came up after him, the people themselves also, playing with flutes, and rejoicing with great joy, —so that the earth rent with the sound of them.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 And Adonijah, and all the guests who were with him, heard it, just as, they, had made an end of eating, —and, when Joab heard the sound of a horn, he said—Wherefore the noise of the city, in tumult?
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 While yet he was speaking, lo! Jonathan son of Abiathar the priest, came in, —and Adonijah said—Come in, for, a worthy man, thou art, and, good tidings, dost thou bring.
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 But Jonathan responded and said to Adonijah, —Of a truth, our lord, King David, hath made, Solomon, king.
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 And the king hath sent with him—Zadok the priest, and Nathan the prophet, and Benaiah son of Jehoiada, with the Cherethites, and the Pelethites, —and they have caused him to ride upon the mule of the king;
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 and Zadok the priest and Nathan the prophet have anointed him king, in Gihon, and they went up from thence rejoicing, so that the city rang again, —That, is the noise ye have heard.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 Moreover also, Solomon hath taken his seat upon the throne of the kingdom.
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Moreover also, the servants of the king have been in, to bless our lord King David, saying—Thy God make the name of Solomon better than thy name, and make his throne greater than thy throne, —And the king bowed himself upon his bed.
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 Moreover also, thus and thus, hath said the king, —Blessed be Yahweh, God of Israel, who hath given, to-day, one to sit upon my throne, mine own eyes also beholding it.
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Then trembled and rose up, all Adonijah’s guests, —and departed, every man his own way.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Adonijah also, feared because of Solomon, —and rose and went, and caught hold of the horns of the altar.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 And it was told Solomon, saying, Lo! Adonijah, feareth King Solomon, —lo! therefore, he hath laid hold of the horns of the altar, saying, Let King Solomon swear unto me at once that he will not put his servant to death with the sword.
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Then said Solomon, If he will be a man of worth, there shall not one hair of him fall to the earth, —but, if mischief be found in him, then shall he die.
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 So King Solomon sent, and brought him down from the altar, and he came in, and bowed himself down to King Solomon, —and Solomon said unto him—Go to thine own house.
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< 1 Kings 1 >