< Psalms 88 >

1 A Song, a Psalm of the sons of Korah; for the Chief Musician; set to Mahalath Leannoth. Maschil of Heman the Ezrahite. O LORD, the God of my salvation, I have cried day and night before thee:
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Let my prayer enter into thy presence; incline thine ear unto my cry:
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 For my soul is full of troubles, and my life draweth nigh unto Sheol. (Sheol h7585)
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
4 I am counted with them that go down into the pit; I am as a man that hath no help:
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 Cast off among the dead, like the slain that lie in the grave, whom thou rememberest no more; and they are cut off from thy hand.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Thou hast laid me in the lowest pit, in dark places, in the deeps.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 Thy wrath lieth hard upon me, and thou hast afflicted me with all thy waves. (Selah)
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Thou hast put mine acquaintance far from me; thou hast made me an abomination unto them: I am shut up, and I cannot come forth.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 Mine eye wasteth away by reason of affliction: I have called daily upon thee, O LORD, I have spread forth my hands unto thee.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Wilt thou shew wonders to the dead? shall they that are deceased arise and praise thee? (Selah)
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 Shall thy lovingkindness be declared in the grave? or thy faithfulness in Destruction?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Shall thy wonders be known in the dark? and thy righteousness in the land of forgetfulness?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 But unto thee, O LORD, have I cried, and in the morning shall my prayer come before thee.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 LORD, why castest thou off my soul? why hidest thou thy face from me?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 I am afflicted and ready to die from my youth up: while I suffer thy terrors I am distracted.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Thy fierce wrath is gone over me; thy terrors have cut me off.
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 They came round about me like water all the day long; they compassed me about together.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 Lover and friend hast thou put far from me, and mine acquaintance into darkness.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

< Psalms 88 >