< Psalms 73 >
1 A Psalm of Asaph. Surely God is good to Israel, [even] to such as are pure in heart.
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 But as for me, my feet were almost gone; my steps had well nigh slipped.
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 For I was envious at the arrogant, when I saw the prosperity of the wicked.
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 For there are no bands in their death: but their strength is firm.
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 They are not in trouble as [other] men; neither are they plagued like [other] men.
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 Therefore pride is as a chain about their neck; violence covereth them as a garment.
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 Their eyes stand out with fatness: they have more than heart could wish.
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 They scoff, and in wickedness utter oppression: they speak loftily.
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 They have set their mouth in the heavens, and their tongue walketh through the earth.
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 Therefore his people return hither: and waters of a full [cup] are wrung out by them.
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 And they say, How doth God know? and is there knowledge in the Most High?
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Behold, these are the wicked; and, being alway at ease, they increase in riches.
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Surely in vain have I cleansed my heart, and washed my hands in innocency;
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 For all the day long have I been plagued, and chastened every morning.
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 If I had said, I will speak thus; behold, I had dealt treacherously with the generation of thy children.
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 When I thought how I might know this, it was too painful for me;
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 Until I went into the sanctuary of God, and considered their latter end.
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Surely thou settest them in slippery places: thou castest them down to destruction.
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 How are they become a desolation in a moment! they are utterly consumed with terrors.
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 As a dream when one awaketh; so, O Lord, when thou awakest, thou shalt despise their image.
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 For my heart was grieved, and I was pricked in my reins:
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 So brutish was I, and ignorant; I was [as] a beast before thee.
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 Nevertheless I am continually with thee: thou hast holden my right hand.
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Thou shalt guide me with thy counsel, and afterward receive me to glory.
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Whom have I in heaven [but thee]? and there is none upon earth that I desire beside thee.
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 My flesh and my heart faileth: [but] God is the strength of my heart and my portion for ever.
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 For, lo, they that are far from thee shall perish: thou hast destroyed all them that go a whoring from thee.
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 But it is good for me to draw near unto God: I have made the Lord GOD my refuge, that I may tell of all thy works.
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.