< Psalms 49 >

1 For the Chief Musician; a Psalm of the sons of Korah. Hear this, all ye peoples; give ear, all ye inhabitants of the world:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 Both low and high, rich and poor together.
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 My mouth shall speak wisdom; and the meditation of my heart shall be of understanding.
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 I will incline mine ear to a parable: I will open my dark saying upon the harp.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Wherefore should I fear in the days of evil, when iniquity at my heels compasseth me about?
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 They that trust in their wealth, and boast themselves in the multitude of their riches;
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 None [of them] can by any means redeem his brother, nor give to God a ransom for him:
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 (For the redemption of their soul is costly, and must be let alone for ever: )
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 That he should still live alway, that he should not see corruption.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 For he seeth that wise men die, the fool and the brutish together perish, and leave their wealth to others.
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 Their inward thought is, [that] their houses [shall continue] for ever, [and] their dwelling places to all generations; they call their lands after their own names.
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 But man abideth not in honour: he is like the beasts that perish.
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 This their way is their folly: yet after them men approve their sayings. (Selah)
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 They are appointed as a flock for Sheol; death shall be their shepherd: and the upright shall have dominion over them in the morning; and their beauty shall be for Sheol to consume, that there be no habitation for it. (Sheol h7585)
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
15 But God will redeem my soul from the power of Sheol: for he shall receive me. (Selah) (Sheol h7585)
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
16 Be not thou afraid when one is made rich, when the glory of his house is increased:
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 For when he dieth he shall carry nothing away; his glory shall not descend after him.
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 Though while he lived he blessed his soul, and men praise thee, when thou doest well to thyself,
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 He shall go to the generation of his fathers; they shall never see the light.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 Man that is in honour, and understandeth not, is like the beasts that perish.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.

< Psalms 49 >