< Psalms 2 >
1 Why do the nations rage, and the peoples imagine a vain thing?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 The kings of the earth set themselves, and the rulers take counsel together, against the LORD, and against his anointed, [saying],
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Let us break their bands asunder, and cast away their cords from us.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 He that sitteth in the heavens shall laugh: the Lord shall have them in derision.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Then shall he speak unto them in his wrath, and vex them in his sore displeasure:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 Yet I have set my king upon my holy hill of Zion.
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 I will tell of the decree: the LORD said unto me, Thou art my son; this day have I begotten thee.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Ask of me, and I will give thee the nations for thine inheritance, and the uttermost parts of the earth for thy possession.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Thou shalt break them with a rod of iron; thou shalt dash them in pieces like a potter’s vessel.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Now therefore be wise, O ye kings: be instructed, ye judges of the earth.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Serve the LORD with fear, and rejoice with trembling.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Kiss the son, lest he be angry, and ye perish in the way, for his wrath will soon be kindled. Blessed are all they that put their trust in him.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.