< Psalms 111 >

1 Praise ye the LORD. I will give thanks unto the LORD with my whole heart, in the council of the upright, and in the congregation.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 The works of the LORD are great, sought out of all them that have pleasure therein.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 His work is honour and majesty: and his righteousness endureth for ever.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 He hath made his wonderful works to be remembered: the LORD is gracious and full of compassion.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 He hath given meat unto them that fear him: he will ever be mindful of his covenant.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 He hath shewed his people the power of his works, in giving them the heritage of the nations.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 The works of his hands are truth and judgment; all his precepts are sure.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 They are established for ever and ever, they are done in truth and uprightness.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 He hath sent redemption unto his people; he hath commanded his covenant for ever: holy and reverend is his name.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 The fear of the LORD is the beginning of wisdom; a good understanding have all they that do thereafter: his praise endureth for ever.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Psalms 111 >