< Psalms 109 >
1 For the Chief Musician. A Psalm of David. Hold not thy peace, O God of my praise;
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 For the mouth of the wicked and the mouth of deceit have they opened against me: they have spoken unto me with a lying tongue.
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 They compassed me about also with words of hatred, and fought against me without a cause.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 For my love they are my adversaries: but I [give myself unto] prayer.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 And they have rewarded me evil for good, and hatred for my love.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Set thou a wicked man over him: and let an adversary stand at his right hand.
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 When he is judged, let him come forth guilty; and let his prayer be turned into sin.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Let his days be few; [and] let another take his office.
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Let his children be fatherless, and his wife a widow.
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Let his children be vagabonds, and beg; and let them seek [their bread] out of their desolate places.
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Let the extortioner catch all that he hath; and let strangers make spoil of his labour.
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Let there be none to extend mercy unto him; neither let there be any to have pity on his fatherless children.
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Let his posterity be cut off; in the generation following let their name be blotted out.
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Let the iniquity of his fathers be remembered with the LORD; and let not the sin of his mother be blotted out.
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Let them be before the LORD continually, that he may cut off the memory of them from the earth.
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Because that he remembered not to shew mercy, but persecuted the poor and needy man, and the broken in heart, to slay [them].
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Yea, he loved cursing, and it came unto him; and he delighted not in blessing, and it was far from him.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 He clothed himself also with cursing as with his garment, and it came into his inward parts like water, and like oil into his bones. Let it be unto him as the raiment
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 wherewith he covereth himself, and for the girdle wherewith he is girded continually.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 This is the reward of mine adversaries from the LORD, and of them that speak evil against my soul.
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 But deal thou with me, O GOD the Lord, for thy name’s sake: because thy mercy is good, deliver thou me,
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 For I am poor and needy, and my heart is wounded within me.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 I am gone like the shadow when it declineth: I am tossed up and down as the locust.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 My knees are weak through fasting; and my flesh faileth of fatness.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 I am become also a reproach unto them: when they see me, they shake their head.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Help me, O LORD my God; O save me according to thy mercy:
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 That they may know that this is thy hand; [that] thou, LORD, hast done it.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Let them curse, but bless thou: when they arise, they shall be ashamed, but thy servant shall rejoice.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Let mine adversaries be clothed with dishonour, and let them cover themselves with their own shame as with a mantle.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 I will give great thanks unto the LORD with my mouth; yea, I will praise him among the multitude.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 For he shall stand at the right hand of the needy, to save him from them that judge his soul.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.