< Psalms 100 >
1 A Psalm of thanksgiving. Make a joyful noise unto the LORD, all ye lands.
Salimo. Nyimbo yothokoza. Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.
2 Serve the LORD with gladness: come before his presence with singing.
Mulambireni Yehova mosangalala; bwerani pamaso pake ndi nyimbo zachikondwerero.
3 Know ye that the LORD he is God: it is he that hath made us, and we are his; we are his people, and the sheep of his pasture.
Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu. Iye ndiye amene anatipanga ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake, nkhosa za pabusa pake.
4 Enter into his gates with thanksgiving, and into his courts with praise: give thanks unto him, and bless his name.
Lowani ku zipata zake ndi chiyamiko ndi ku mabwalo ake ndi matamando; muyamikeni ndi kutamanda dzina lake.
5 For the LORD is good; his mercy [endureth] for ever; and his faithfulness unto all generations.
Pakuti Yehova ndi wabwino ndipo chikondi chake ndi chamuyaya; kukhulupirika kwake nʼkokhazikika pa mibado ndi mibado.