< Psalms 10 >
1 Why standest thou afar off, O LORD? why hidest thou thyself in times of trouble?
Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
2 In the pride of the wicked the poor is hotly pursued; let them be taken in the devices that they have imagined.
Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
3 For the wicked boasteth of his heart’s desire, and the covetous renounceth, [yea], contemneth the LORD.
Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
4 The wicked, in the pride of his countenance, [saith], He will not require [it]. All his thoughts are, There is no God.
Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
5 His ways are firm at all times; thy judgments are far above out of his sight: as for all his adversaries, he puffeth at them.
Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
6 He saith in his heart, I shall not be moved: to all generations I shall not be in adversity.
Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
7 His mouth is full of cursing and deceit and oppression: under his tongue is mischief and iniquity.
Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
8 He sitteth in the lurking places of the villages: in the covert places doth he murder the innocent: his eyes are privily set against the helpless.
Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
9 He lurketh in the covert as a lion in his den: he lieth in wait to catch the poor: he doth catch the poor, when he draweth him in his net.
Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
10 He croucheth, he boweth down, and the helpless fall by his strong ones.
Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
11 He saith in his heart, God hath forgotten: he hideth his face; he will never see it.
Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
12 Arise, O LORD; O God, lift up thine hand: forget not the poor.
Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
13 Wherefore doth the wicked contemn God, and say in his heart, Thou wilt not require [it]?
Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
14 Thon hast seen [it]; for thou beholdest mischief and spite, to take it into thy hand: the helpless committeth [himself] unto thee; thou hast been the helper of the fatherless.
Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
15 Break thou the arm of the wicked; and as for the evil man, seek out his wickedness till thou find none.
Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
16 The LORD is King for ever and ever: the nations are perished out of his land.
Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
17 LORD, thou hast heard the desire of the meek: thou wilt prepare their heart, thou wilt cause thine ear to hear:
Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
18 To judge the fatherless and the oppressed, that man which is of the earth may be terrible no more.
Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.