< Proverbs 6 >
1 My son, if thou art become surety for thy neighbour, if thou hast stricken thy hands for a stranger,
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 Thou art snared with the words of thy mouth, thou art taken with the words of thy mouth.
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 Do this now, my son, and deliver thyself, seeing thou art come into the hand of thy neighbour; go, humble thyself, and importune thy neighbour.
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 Give not sleep to thine eyes, nor slumber to thine eyelids.
Usagone tulo, usawodzere.
5 Deliver thyself as a roe from the hand [of the hunter], and as a bird from the hand of the fowler.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Go to the ant, thou sluggard; consider her ways, and be wise:
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 Which having no chief, overseer, or ruler,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 Provideth her meat in the summer, and gathereth her food in the harvest.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 How long wilt thou sleep, O sluggard? when wilt thou arise out of thy sleep?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 [Yet] a little sleep, a little slumber, a little folding of the hands to sleep:
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 So shall thy poverty come as a robber, and thy want as an armed man.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 A worthless person, a man of iniquity; he walketh with a froward mouth;
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 He winketh with his eyes, he speaketh with his feet, he maketh signs with his fingers;
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 Frowardness is in his heart, he deviseth evil continually; he soweth discord.
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Therefore shall his calamity come suddenly; on a sudden shall he be broken and that without remedy.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 There be six things which the LORD hateth; yea, seven which are an abomination unto him:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 Haughty eyes, a lying tongue, and hands that shed innocent blood;
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 An heart that deviseth wicked imaginations, feet that be swift in running to mischief;
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 A false witness that uttereth lies, and he that soweth discord among brethren.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 My son, keep the commandment of thy father, and forsake not the law of thy mother:
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 Bind them continually upon thine heart, tie them about thy neck.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 When thou walkest, it shall lead thee; when thou sleepest, it shall watch over thee; and when thou awakest, it shall talk with thee.
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 For the commandment is a lamp; and the law is light; and reproofs of instruction are the way of life:
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 To keep thee from the evil woman, from the flattery of the stranger’s tongue.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Lust not after her beauty in thine heart; neither let her take thee with her eyelids.
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 For on account of a whorish woman [a man is brought] to a piece of bread: and the adulteress hunteth for the precious life.
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Can a man take fire in his bosom, and his clothes not be burned?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Or can one walk upon hot coals, and his feet not be scorched?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 So he that goeth in to his nieghbour’s wife; whosoever toucheth her shall not be unpunished.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Men do not despise a thief, if he steal to satisfy his soul when he is hungry:
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 But if he be found, he shall restore sevenfold; he shall give all the substance of his house.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 He that committeth adultery with a woman is void of understanding: he doeth it that would destroy his own soul.
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 Wounds and dishonour shall he get; and his reproach shall not be wiped away.
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 For jealousy is the rage of a man; and he will not spare in the day of vengeance.
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 He will not regard any ransom; neither will he rest content, though thou givest many gifts.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.