< Proverbs 11 >

1 A FALSE balance is an abomination to the LORD: but a just weight is his delight.
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera.
2 When pride cometh, then cometh shame: but with the lowly is wisdom.
Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi, koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.
3 The integrity of the upright shall guide them: but the perverseness of the treacherous shall destroy them.
Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera, koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.
4 Riches profit not in the day of wrath: but righteousness delivereth from death.
Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
5 The righteousness of the perfect shall direct his way: but the wicked shall fall by his own wickedness.
Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo, koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.
6 The righteousness of the upright shall deliver them: but they that deal treacherously shall be taken in their own mischief.
Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa, koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.
7 When a wicked man dieth [his] expectation shall perish: and the hope of iniquity perisheth.
Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso. Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.
8 The righteous is delivered out of trouble, and the wicked cometh in his stead.
Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto, koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.
9 With his mouth the godless man destroyeth his neighbour: but through knowledge shall the righteous be delivered.
Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake, koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.
10 When it goeth well with the righteous, the city rejoiceth: and when the wicked perish, there is shouting.
Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera, ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.
11 By the blessing of the upright the city is exalted: but it is overthrown by the mouth of the wicked.
Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima, koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.
12 He that despiseth his neighbour is void of wisdom: but a man of understanding holdeth his peace.
Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru, koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.
13 He that goeth about as a talebearer revealeth secrets: but he that is of a faithful spirit concealeth the matter.
Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi; koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.
14 Where no wise guidance is, the people falleth: but in the multitude of counsellors there is safety.
Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa; koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.
15 He that is surety for a stranger shall smart for it: but he that hateth suretiship is sure.
Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto, koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.
16 A gracious woman retaineth honour: and violent men retain riches.
Mkazi wodekha amalandira ulemu, koma amuna ankhanza amangopata chuma.
17 The merciful man doeth good to his own soul: but he that is cruel troubleth his own flesh.
Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.
18 The wicked earneth deceitful wages: but he that soweth righteousness [hath] a sure reward.
Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu, koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.
19 He that is stedfast in righteousness [shall attain] unto life: and he that pursueth evil [doeth it] to his own death.
Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo, koma wothamangira zoyipa adzafa.
20 They that are perverse in heart are an abomination to the LORD: but such as are perfect in [their] way are his delight.
Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.
21 [Though] hand [join] in hand, the evil man shall not be unpunished: but the seed of the righteous shall be delivered.
Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa, koma anthu olungama adzapulumuka.
22 [As a] jewel of gold in a swine’s snout, [so is] a fair woman which is without discretion.
Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba, ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.
23 The desire of the righteous is only good: [but] the expectation of the wicked is wrath.
Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha, koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.
24 There is that scattereth, and increaseth yet more; and there is that withholdeth more than is meet, but [it tendeth] only to want.
Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe; wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.
25 The liberal soul shall be made fat: and he that watereth shall be watered also himself.
Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera; iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.
26 He that withholdeth corn, the people shall curse him: but blessing shall be upon the head of him that selleth it.
Anthu amatemberera womana anzake chakudya, koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.
27 He that diligently seeketh good seeketh favour: but he that searcheth after mischief, it shall come unto him.
Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo, koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.
28 He that trusteth in his riches shall fall: but the righteous shall flourish as the green leaf.
Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota, koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.
29 He that troubleth his own house shall inherit the wind: and the foolish shall be servant to the wise of heart.
Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto, ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.
30 The fruit of the righteous is a tree of life; and he that is wise winneth souls.
Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo, ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.
31 Behold, the righteous shall be recompensed in the earth: how much more the wicked and the sinner!
Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi, kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!

< Proverbs 11 >