< Numbers 26 >
1 And it came to pass after the plague, that the LORD spake unto Moses and unto Eleazar the son of Aaron the priest, saying,
Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
2 Take the sum of all the congregation of the children of Israel, from twenty years old and upward, by their fathers’ houses, all that are able to go forth to war in Israel.
“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
3 And Moses and Eleazar the priest spake with them in the plains of Moab by the Jordan at Jericho, saying,
Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
4 [Take the sum of the people], from twenty years old and upward; as the LORD commanded Moses and the children of Israel, which came forth out of the land of Egypt.
“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
5 Reuben, the firstborn of Israel: the sons of Reuben; [of] Hanoch, the family of the Hanochites: of Pallu, the family of the Palluites:
Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
6 of Hezron, the family of the Hezronites: of Carmi, the family of the Carmites.
kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
7 These are the families of the Reubenites: and they that were numbered of them were forty and three thousand and seven hundred and thirty.
Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
8 And the sons of Pallu; Eliab.
Mwana wa Palu anali Eliabu,
9 And the sons of Eliab; Nemuel, and Dathan, and Abiram. These are that Dathan and Abiram, which were called of the congregation, who strove against Moses and against Aaron in the company of Korah, when they strove against the LORD:
ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
10 and the earth opened her mouth, and swallowed them up together with Korah, when that company died; what time the fire devoured two hundred and fifty men, and they became a sign.
Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
11 Notwithstanding the sons of Korah died not.
Koma ana a Kora sanafe nawo.
12 The sons of Simeon after their families: of Nemuel, the family of the Nemuelites: of Jamin, the family of the Jaminites: of Jachin, the family of the Jachinites:
Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
13 of Zerah, the family of the Zerahites: of Shaul, the family of the Shaulites.
kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
14 These are the families of the Simeonites, twenty and two thousand and two hundred.
Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
15 The sons of Gad after their families: of Zephon, the family of the Zephonites: of Haggi, the family of the Haggites: of Shuni, the family of the Shunites:
Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
16 of Ozni, the family of the Oznites: of Eri, the family of the Erites:
kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
17 of Arod, the family of the Arodites: of Areli, the family of the Arelites.
kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
18 These are the families of the sons of Gad according to those that were numbered of them, forty thousand and five hundred.
Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
19 The sons of Judah, Er and Onan: and Er and Onan died in the land of Canaan.
Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
20 And the sons of Judah after their families were; of Shelah, the family of the Shelanites: of Perez, the family of the Perezites: of Zerah, the family of the Zerahites.
Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
21 And the sons of Perez were; of Hezron, the family of the Hezronites: of Hamul, the family of the Hamulites.
Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
22 These are the families of Judah according to those that were numbered of them, threescore and sixteen thousand and five hundred.
Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
23 The sons of Issachar after their families: [of] Tola, the family of the Tolaites: of Puvah, the family of the Punites:
Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
24 of Jashub, the family of the Jashubites: of Shimron, the family of the Shimronites.
kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
25 These are the families of Issachar according to those that were numbered of them, threescore and four thousand and three hundred.
Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
26 The sons of Zebulun after their families: of Sered, the family of the Seredites: of Elon, the family of the Elonites: of Jahleel, the family of the Jahleelites.
Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
27 These are the families of the Zebulunites according to those that were numbered of them, threescore thousand and five hundred.
Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
28 The sons of Joseph after their families: Manasseh and Ephraim.
Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
29 The sons of Manasseh: of Machir, the family of the Machirites: and Machir begat Gilead: of Gilead, the family of the Gileadites.
Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
30 These are the sons of Gilead: [of] Iezer, the family of the Iezerites: of Helek, the family of the Helekites:
Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
31 and [of] Asriel, the family of the Asrielites: and [of] Shechem, the family of the Shechemites:
kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
32 and [of] Shemida, the family of the Shemidaites: and [of] Hepher, the family of the Hepherites.
kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
33 And Zelophehad the son of Hepher had no sons, but daughters: and the names of the daughters of Zelophehad were Mahlah, and Noah, Hoglah, Milcah, and Tirzah.
(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
34 These are the families of Manasseh: and they that were numbered of them were fifty and two thousand and seven hundred.
Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
35 These are the sons of Ephraim after their families: of Shuthelah, the family of the Shuthelahites: of Becher, the family of the Becherites: of Tahan, the family of the Tahanites.
Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
36 And these are the sons of Shuthelah: of Eran, the family of the Eranites.
Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
37 These are the families of the sons of Ephraim according to those that were numbered of them, thirty and two thousand and five hundred. These are the sons of Joseph after their families.
Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
38 The sons of Benjamin after their families: of Bela, the family of the Belaites: of Ashbel, the family of the Ashbelites: of Ahiram, the family of the Ahiramites:
Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
39 of Shephupham, the family of the Shuphamites: of Hupham, the family of the Huphamites.
kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
40 And the sons of Bela were Ard and Naaman: [of Ard], the family of the Ardites: of Naaman, the family of the Naamites.
Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
41 These are the sons of Benjamin after their families: and they that were numbered of them were forty and five thousand and six hundred.
Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
42 These are the sons of Dan after their families: of Shuham, the family of the Shuhamites. These are the families of Dan after their families.
Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
43 All the families of the Shuhamites, according to those that were numbered of them, were threescore and four thousand and four hundred.
Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
44 The sons of Asher after their families: of Imnah, the family of the Imnites: of Ishvi, the family of the Ishvites: of Beriah, the family of the Beriites.
Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
45 Of the sons of Beriah: of Heber, the family of the Heberites: of Malchiel, the family of the Malchielites.
ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
46 And the name of the daughter of Asher was Serah.
(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
47 These are the families of the sons of Asher according to those that were numbered of them, fifty and three thousand and four hundred.
Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
48 The sons of Naphtali after their families: of Jahzeel, the family of the Jahzeelites: of Guni, the family of the Gunites:
Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
49 of Jezer, the family of the Jezerites: of Shillem, the family of the Shillemites.
kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
50 These are the families of Naphtali according to their families: and they that were numbered of them were forty and five thousand and four hundred.
Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
51 These are they that were numbered of the children of Israel, six hundred thousand and a thousand seven hundred and thirty.
Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
52 And the LORD spake unto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
53 Unto these the land shall be divided for an inheritance according to the number of names.
“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
54 To the more thou shalt give the more inheritance, and to the fewer thou shalt give the less inheritance: to every one according to those that were numbered of him shall his inheritance be given.
Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
55 Notwithstanding the land shall be divided by lot: according to the names of the tribes of their fathers they shall inherit.
Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
56 According to the lot shall their inheritance be divided between the more and the fewer.
Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
57 And these are they that were numbered of the Levites after their families: of Gershon, the family of the Gershonites: of Kohath, the family of the Kohathites: of Merari, the family of the Merarites.
Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
58 These are the families of Levi: the family of the Libnites, the family of the Hebronites, the family of the Mahlites, the family of the Mushites, the family of the Korahites. And Kohath begat Amram.
Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
59 And the name of Amram’s wife was Jochebed, the daughter of Levi, who was born to Levi in Egypt: and she bare unto Amram Aaron and Moses, and Miriam their sister.
Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
60 And unto Aaron were born Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar.
Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
61 And Nadab and Abihu died, when they offered strange fire before the LORD.
Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
62 And they that were numbered of them were twenty and three thousand, every male from a month old and upward: for they were not numbered among the children of Israel, because there was no inheritance given them among the children of Israel.
Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
63 These are they that were numbered by Moses and Eleazar the priest; who numbered the children of Israel in the plains of Moab by the Jordan at Jericho.
Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
64 But among these there was not a man of them that were numbered by Moses and Aaron the priest; who numbered the children of Israel in the wilderness of Sinai.
Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
65 For the LORD had said of them, They shall surely die in the wilderness. And there was not left a man of them, save Caleb the son of Jephunneh, and Joshua the son of Nun.
Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.