< John 9 >

1 And as he passed by, he saw a man blind from his birth.
Iye akuyendabe, anaona munthu wosaona chibadwire.
2 And his disciples asked him, saying, Rabbi, who did sin, this man, or his parents, that he should be born blind?
Ophunzira ake anamufunsa Iye kuti, “Rabi anachimwa ndani, munthuyu kapena makolo ake, kuti iye abadwe wosaona?”
3 Jesus answered, Neither did this man sin, nor his parents: but that the works of God should be made manifest in him.
Yesu anayankha kuti, “Sikuti iyeyu anachimwa kapena makolo ake, koma izi zinachitika kuti Mulungu aonetse ntchito zake mwa iyeyu.
4 We must work the works of him that sent me, while it is day: the night cometh, when no man can work.
Ife tiyenera kugwira ntchito za Iye amene anandituma kukanali masana. Usiku ukubwera, pamene wina aliyense sadzagwira ntchito.
5 When I am in the world, I am the light of the world.
Pamene Ine ndili mʼdziko lapansi, Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi.”
6 When he had thus spoken, he spat on the ground, and made clay of the spittle, and anointed his eyes with the clay,
Atanena izi, Iye anathira malovu pansi ndi kukanda dothi, napaka matopewo mʼmaso a munthuyo.
7 and said unto him, Go, wash in the pool of Siloam (which is by interpretation, Sent). He went away therefore, and washed, and came seeing.
Yesu anamuwuza iye kuti, “Pita kasambe mʼdziwe la Siloamu” (mawu awa akutanthauza Wotumidwa). Choncho munthuyo anapita ndi kukasamba ndipo anabwerako akupenya.
8 The neighbours therefore, and they which saw him aforetime, that he was a beggar, said, Is not this he that sat and begged?
Anzake ndi iwo amene anamuona iye poyamba akupempha anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene amapemphapempha uja?”
9 Others said, It is he: others said, No, but he is like him. He said, I am [he].
Ena ananena kuti anali yemweyo. Ena anati, “Ayi, sakuoneka ngati yemweyo.” Koma iye mwini ananenetsa kuti, “Munthuyo ndine.”
10 They said therefore unto him, How then were thine eyes opened?
Iwo anafunsitsa kuti, “Kodi nanga maso ako anatsekuka bwanji?”
11 He answered, The man that is called Jesus made clay, and anointed mine eyes, and said unto me, Go to Siloam, and wash: so I went away and washed, and I received sight.
Iye anayankha kuti, “Munthu wina wotchedwa Yesu anakanda dothi ndi kupaka mʼmaso anga. Iye anandiwuza kuti ndipite ku Siloamu ndi kukasamba. Choncho ndinapita kukasamba, ndipo ndikuona.”
12 And they said unto him, Where is he? He saith, I know not.
Iwo anamufunsa iye kuti, “Ali kuti munthu ameneyu?” Iye anati, “Ine sindikudziwa.”
13 They bring to the Pharisees him that aforetime was blind.
Iwo anabwera naye munthu amene poyamba anali wosaona kwa Afarisi.
14 Now it was the sabbath on the day when Jesus made the clay, and opened his eyes.
Tsono linali la Sabata tsiku limene Yesu anakanda dothi ndi kutsekula maso a munthuyu.
15 Again therefore the Pharisees also asked him how he received his sight. And he said unto them, He put clay upon mine eyes, and I washed, and do see.
Choncho Afarisi anamufunsanso iye momwe analandirira kuona kwake. Munthuyo anayankha kuti, “Iye anapaka matope mʼmaso anga, ndipo ine ndinakasamba, ndipo ndikuona.”
16 Some therefore of the Pharisees said, This man is not from God, because he keepeth not the sabbath. But others said, How can a man that is a sinner do such signs? And there was a division among them.
Ena a Afarisi anati, “Munthu uyu siwochokera kwa Mulungu, pakuti sasunga Sabata.” Koma enanso anafunsa kuti, “Kodi munthu wochimwa angachite bwanji zizindikiro zodabwitsa ngati izi?” Choncho iwo anagawanika.
17 They say therefore unto the blind man again, What sayest thou of him, in that he opened thine eyes? And he said, He is a prophet.
Pomaliza iwo anatembenukiranso kwa munthu amene anali wosaona uja nati, “Kodi iwe unena chiyani za Iye poti ndi maso ako amene watsekula?” Munthuyo anayankha kuti, “Iye ndi mneneri.”
18 The Jews therefore did not believe concerning him, that he had been blind, and had received his sight, until they called the parents of him that had received his sight,
Ayuda sanakhulupirirebe kuti iye anali wosaona ndi kuti anayamba kuona kufikira atayitana makolo ake.
19 and asked them, saying, Is this your son, who ye say was born blind? how then doth he now see?
Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu ndi mwana wanu? Kodi iyeyu ndi amene mukunena kuti anabadwa wosaona? Nanga zikutheka bwanji kuti akuona?”
20 His parents answered and said, We know that this is our son, and that he was born blind:
Makolo anayankha kuti, “Ife tikudziwa kuti ndi mwana wathu, ndipo tikudziwa kuti anabadwa wosaona.
21 but how he now seeth, we know not; or who opened his eyes, we know not: ask him; he is of age; he shall speak for himself.
Koma sitidziwa zimene zachitika kuti tsopano azipenya. Amenenso wamupenyetsa sitikumudziwa. Mufunseni ndi wamkulu; iye adziyankhira yekha.”
22 These things said his parents, because they feared the Jews: for the Jews had agreed already, that if any man should confess him [to be] Christ, he should be put out of the synagogue.
Makolo ake ananena izi chifukwa amaopa Ayuda, popeza Ayuda anatsimikiza kale kuti aliyense amene adzamuvomereza Yesu kuti anali Khristu adzatulutsidwa mʼsunagoge.
23 Therefore said his parents, He is of age; ask him.
Ichi ndi chifukwa chake makolo ake anati, “Mufunseni iye ndi wamkulu.”
24 So they called a second time the man that was blind, and said unto him, Give glory to God: we know that this man is a sinner.
Iwo anamuyitanitsa kachiwiri munthu amene anali wosaonayo. Iwo anati, “Lemekeza Mulungu. Ife tikudziwa kuti munthu uyu ndi wochimwa.”
25 He therefore answered, Whether he be a sinner, I know not: one thing I know, that, whereas I was blind, now I see.
Iye anayankha kuti, “Zakuti Iye ndi wochimwa kapena ayi, ine sindikudziwa. Ine ndikudziwa chinthu chimodzi. Ndinali wosaona koma tsopano ndikuona!”
26 They said therefore unto him, What did he to thee? how opened he thine eyes?
Kenaka anamufunsa kuti, “Kodi Iye anachita chiyani kwa iwe? Iye anatsekula motani maso ako?”
27 He answered them, I told you even now, and ye did not hear: wherefore would ye hear it again? would ye also become his disciples?
Iye anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kale ndipo inu simunamvetsetse. Chifukwa chiyani mukufuna mumvenso? Mukufuna kuti inu mukhale ophunzira akenso?”
28 And they reviled him, and said, Thou art his disciple; but we are disciples of Moses.
Pamenepo anamunyoza ndipo anati, “Iwe ndiye ophunzira wa munthuyu! Ife ndife ophunzira a Mose!
29 We know that God hath spoken unto Moses: but as for this man, we know not whence he is.
Ife tikudziwa kuti Mulungu anayankhula kwa Mose, koma za munthu uyu, ife sitikudziwa ngakhale kumene akuchokera.”
30 The man answered and said unto them, Why, herein is the marvel, that ye know not whence he is, and [yet] he opened mine eyes.
Munthuyo anayankha kuti, “Tsopano izi ndi zodabwitsa! Inu simukudziwa kumene akuchokera, komabe iye watsekula maso anga.
31 We know that God heareth not sinners: but if any man be a worshipper of God, and do his will, him he heareth.
Ife tikudziwa kuti Mulungu samvera wochimwa. Iye amamvera munthu woopa Mulungu amene amachita chifuniro chake.
32 Since the world began it was never heard that any one opened the eyes of a man born blind. (aiōn g165)
Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. (aiōn g165)
33 If this man were not from God, he could do nothing.
Ngati munthu uyu akanakhala wosachokera kwa Mulungu, palibe chimene Iye akanachita.”
34 They answered and said unto him, Thou wast altogether born in sins, and dost thou teach us? And they cast him out.
Pamenepo anayankha kuti, “Iwe unabadwa mu uchimo kotheratu; bwanji ukuyesa kutiphunzitsa ife!” Ndipo anamutulutsa kunja.
35 Jesus heard that they had cast him out; and finding him, he said, Dost thou believe on the Son of God?
Yesu anamva kuti anamutulutsa kunja ndipo pamene anamupeza anati, “Kodi ukukhulupirira Mwana wa Munthu?”
36 He answered and said, And who is he, Lord, that I may believe on him?
Munthuyo anafunsa kuti, “Kodi, Ambuye, ameneyo ndi ndani? Ndiwuzeni kuti ndimukhulupirire Iye?”
37 Jesus said unto him, Thou hast both seen him, and he it is that speaketh with thee.
Yesu anati, “Iwe wamuona tsopano. Zoonadi ndiye amene akuyankhula nawe.”
38 And he said, Lord, I believe. And he worshipped him.
Pamenepo munthuyo anati, “Ambuye, ndikukhulupirira,” ndipo anamulambira Iye.
39 And Jesus said, For judgment came I into this world, that they which see not may see; and that they which see may become blind.
Yesu anati, “Ndinabwera pansi pano kudzaweruza kuti osaona aone ndi openya asaone.”
40 Those of the Pharisees which were with him heard these things, and said unto him, Are we also blind?
Afarisi ena amene anali pafupi naye anamva akunena izi ndipo anafunsa kuti, “Chiyani? Kodi ndife osaonanso?”
41 Jesus said unto them, If ye were blind, ye would have no sin: but now ye say, We see: your sin remaineth.
Yesu anati, “Mukanakhala osaona, simukanachimwa; koma tsopano popeza mukuti mumaona, ndinu ochimwabe.”

< John 9 >