< Job 7 >

1 Is there not a warfare to man upon earth? and are not his days like the days of an hireling?
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 As a servant that earnestly desireth the shadow, and as an hireling that looketh for his wages:
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 So am I made to possess months of vanity, and wearisome nights are appointed to me.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 When I lie down, I say, When shall I arise? but the night is long; and I am full of tossings to and fro unto the dawning of the day.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 My flesh is clothed with worms and clods of dust; my skin closeth up and breaketh out afresh.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 My days are swifter than a weaver’s shuttle, and are spent without hope.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 Oh remember that my life is wind: mine eye shall no more see good.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 The eye of him that seeth me shall behold me no more: thine eyes shall be upon me, but I shall not be.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 As the cloud is consumed and vanisheth away, so he that goeth down to Sheol shall come up no more. (Sheol h7585)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
10 He shall return no more to his house, neither shall his place know him any more.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Therefore I will not refrain my mouth; I will speak in the anguish of my spirit; I will complain in the bitterness of my soul.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Am I a sea, or a sea-monster, that thou settest a watch over me?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 When I say, My bed shall comfort me, my couch shall ease my complaint;
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 Then thou scarest me with dreams, and terrifiest me through visions:
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 So that my soul chooseth strangling, and death rather than [these] my bones.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 I loathe [my life]; I would not live alway: let me alone; for my days are vanity.
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 What is man, that thou shouldest magnify him, and that thou shouldest set thine heart upon him,
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 And that thou shouldest visit him every morning, and try him every moment?
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 How long wilt thou not look away from me, nor let me alone till I swallow down my spittle?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 If I have sinned, what do I unto thee, O thou watcher of men? why hast thou set me as a mark for thee, so that I am a burden to myself?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 And why dost thou not pardon my transgression, and take away mine iniquity? for now shall I lie down in the dust; and thou shall seek me diligently, but I shall not be.
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

< Job 7 >