< Job 29 >
1 And Job again took up his parable, and said,
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Oh that I were as in the months of old, as in the days when God watched over me;
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 When his lamp shined upon my head, and by his light I walked through darkness;
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 As I was in the ripeness of my days, when the secret of God was upon my tent;
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 When the Almighty was yet with me, and my children were about me;
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 When my steps were washed with butter, and the rock poured me out rivers of oil!
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 When I went forth to the gate unto the city, when I prepared my seat in the street,
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 The young men saw me and hid themselves, and the aged rose up and stood;
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 The princes refrained talking, and laid their hand on their mouth;
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 The voice of the nobles was hushed, and their tongue cleaved to the roof of their mouth.
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 For when the ear heard [me], then it blessed me; and when the eye saw [me], it gave witness unto me:
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 Because I delivered the poor that cried, the fatherless also, that had none to help him.
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 The blessing of him that was ready to perish came upon me: and I caused the widow’s heart to sing for joy.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 I put on righteousness, and it clothed me: my justice was as a robe and a diadem.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 I was eyes to the blind, and feet was I to the lame.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 I was a father to the needy: and the cause of him that I knew not I searched out.
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 And I brake the jaws of the unrighteous, and plucked the prey out of his teeth.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 Then I said, I shall die in my nest, and I shall multiply my days as the sand:
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 My root is spread out to the waters, and the dew lieth all night upon my branch:
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 My glory is fresh in me, and my bow is renewed in my hand.
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 Unto me men gave ear, and waited, and kept silence for my counsel.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 After my words they spake not again; and my speech dropped upon them.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 And they waited for me as for the rain; and they opened their mouth wide as for the latter rain.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 If I laughed on them, they believed [it] not; and the light of my countenance they cast not down.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 I chose out their way, and sat [as] chief, and dwelt as a king in the army, as one that comforteth the mourners.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”