< Job 27 >
1 And Job again took up his parable, and said,
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 As God liveth, who hath taken away my right; and the Almighty, who hath vexed my soul;
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 (For my life is yet whole in me, and the spirit of God is in my nostrils; )
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 Surely my lips shall not speak unrighteousness, neither shall my tongue utter deceit.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 God forbid that I should justify you: till I die I will not put away mine integrity from me.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 My righteousness I hold fast, and will not let it go: my heart shall not reproach [me] so long as I live.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 Let mine enemy be as the wicked, and let him that riseth up against me be as the unrighteous.
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 For what is the hope of the godless, though he get him gain, when God taketh away his soul?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 Will God hear his cry, when trouble cometh upon him?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Will he delight himself in the Almighty, and call upon God at all times?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 I will teach you concerning the hand of God; that which is with the Almighty will I not conceal.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 Behold, all ye yourselves have seen it; why then are ye become altogether vain?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 This is the portion of a wicked man with God, and the heritage of oppressors, which they receive from the Almighty.
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 If his children be multiplied, it is for the sword; and his offspring shall not be satisfied with bread.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Those that remain of him shall be buried in death, and his widows shall make no lamentation.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Though he heap up silver as the dust, and prepare raiment as the clay;
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 He may prepare it, but the just shall put it on, and the innocent shall divide the silver.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 He buildeth his house as the moth, and as a booth which the keeper maketh.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 He lieth down rich, but he shall not be gathered; he openeth his eyes, and he is not.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Terrors overtake him like waters; a tempest stealeth him away in the night.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 The east wind carrieth him away, and he departeth; and it sweepeth him out of his place.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 For [God] shall hurl at him, and not spare: he would fain flee out of his hand.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 Men shall clap their hands at him, and shall hiss him out of his place.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”