< Job 23 >
1 Then Job answered and said,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Even today is my complaint rebellious: my stroke is heavier than my groaning.
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 Oh that I knew where I might find him, that I might come even to his seat!
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 I would order my cause before him, and fill my mouth with arguments.
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 I would know the words which he would answer me, and understand what he would say unto me.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 Would he contend with me in the greatness of his power? Nay; but he would give heed unto me.
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 There the upright might reason with him; so should I be delivered for ever from my judge.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 Behold, I go forward, but he is not [there]; and backward, but I cannot perceive him:
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 On the left hand, when he doth work, but I cannot behold him: he hideth himself on the right hand, that I cannot see him.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 But he knoweth the way that I take; when he hath tried me, I shall come forth as gold.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 My foot hath held fast to his steps; his way have I kept, and turned not aside.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 I have not gone back from the commandment of his lips; I have treasured up the words of his mouth more than my necessary food.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 But he is in one [mind], and who can turn him? and what his soul desireth, even that he doeth.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 For he performeth that which is appointed for me: and many such things are with him.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Therefore am I troubled at his presence; when I consider, I am afraid of him.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 For God hath made my heart faint, and the Almighty hath troubled me:
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 Because I was not cut off before the darkness, neither did he cover the thick darkness from my face.
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.