< Job 17 >

1 My spirit is consumed, my days are extinct, the grave is [ready] for me.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Surely there are mockers with me, and mine eye abideth in their provocation.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Give now a pledge, be surety for me with thyself; who is there that will strike hands with me?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 For thou hast hid their heart from understanding: therefore shalt thou not exalt [them].
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 He that denounceth his friends for a prey, even the eyes of his children shall fail.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 He hath made me also a byword of the people; and I am become an open abhorring.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 Mine eye also is dim by reason of sorrow, and all my members are as a shadow.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Upright men shall be astonied at this, and the innocent shall stir up himself against the godless.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 Yet shall the righteous hold on his way, and he that hath clean hands shall wax stronger and stronger.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 But return ye, all of you, and come now: and I shall not find a wise man among you.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 My days are past, my purposes are broken off, even the droughts of my heart.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 They change the night into a day: the fight, [say they], is near unto the darkness.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 If I look for Sheol as mine house; if I have spread my couch in the darkness; (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 If I have said to corruption, Thou art my father; to the worm, [Thou art] my mother, and my sister;
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 Where then is my hope? and as for my hope, who shall see it?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 It shall go down to the bars of Sheol, when once there is rest in the dust. (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Job 17 >