< Hosea 11 >

1 When Israel was a child, then I loved him, and called my son out of Egypt.
“Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
2 As they called them, so they went from them: they sacrificed unto the Baalim, and burned incense to graven images.
Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
3 Yet I taught Ephraim to go; I took them on my arms; but they knew not that I healed them.
Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
4 I drew them with cords of a man, with bands of love; and I was to them as they that take off the yoke on their jaws, and I laid meat before them.
Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
5 He shall not return into the land of Egypt; but the Assyrian shall be his king, because they refused to return.
“Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
6 And the sword shall fall upon his cities, and shall consume his bars, and devour [them], because of their own counsels.
Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
7 And my people are bent to backsliding from me: though they call them to [him that is] on high, none at all will exalt [him].
Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
8 How shall I give thee up, Ephraim? [how] shall I deliver thee, Israel? how shall I make thee as Admah? [how] shall I set thee as Zeboim? mine heart is turned within me, my compassions are kindled together.
“Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
9 I will not execute the fierceness of mine anger, I will not return to destroy Ephraim: for I am God, and not man; the Holy One in the midst of thee: and I will not enter into the city.
Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
10 They shall walk after the LORD, who shall roar like a lion: for he shall roar, and the children shall come trembling from the west.
Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
11 They shall come trembling as a bird out of Egypt, and as a dove out of the land of Assyria: and I will make them to dwell in their houses, saith the LORD.
Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
12 Ephraim compasseth me about with falsehood, and the house of Israel with deceit: but Judah yet ruleth with God, and is faithful with the Holy One.
Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.

< Hosea 11 >