< 2 Corinthians 6 >

1 And working together [with him] we entreat also that ye receive not the grace of God in vain
Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe.
2 (for he saith, At an acceptable time I hearkened unto thee, And in a day of salvation did I succour thee: behold, now is the acceptable time; behold, now is the day of salvation):
Pakuti akunena kuti, “Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera, ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza. Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”
3 giving no occasion of stumbling in anything, that our ministration be not blamed;
Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke.
4 but in everything commending ourselves, as ministers of God, in much patience, in afflictions, in necessities, in distresses,
Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa.
5 in stripes, in imprisonments, in tumults, in labours, in watchings, in fastings;
Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya;
6 in pureness, in knowledge, in longsuffering, in kindness, in the Holy Ghost, in love unfeigned,
pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi
7 in the word of truth, in the power of God; by the armour of righteousness on the right hand and on the left,
ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo.
8 by glory and dishonour, by evil report and good report; as deceivers, and [yet] true;
Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza.
9 as unknown, and [yet] well known; as dying, and behold, we live; as chastened, and not killed;
Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa.
10 as sorrowful, yet alway rejoicing; as poor, yet making many rich; as having nothing, and [yet] possessing all things.
Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.
11 Our mouth is open unto you, O Corinthians, our heart is enlarged.
Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu.
12 Ye are not straitened in us, but ye are straitened in your own affections.
Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife.
13 Now for a recompense in like kind (I speak as unto [my] children), be ye also enlarged.
Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.
14 Be not unequally yoked with unbelievers: for what fellowship have righteousness and iniquity? or what communion hath light with darkness?
Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima?
15 And what concord hath Christ with Belial? or what portion hath a believer with an unbeliever?
Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira?
16 And what agreement hath a temple of God with idols? for we are a temple of the living God; even as God said, I will dwell in them, and walk in them; and I will be their God, and they shall be my people.
Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti, “Ndidzakhala mwa iwo ndipo ndidzayendayenda pakati pawo, ndipo ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo adzakhala anthu anga.”
17 Wherefore Come ye out from among them, and be ye separate, saith the Lord, And touch no unclean thing; And I will receive you,
Nʼchifukwa chake “Tulukani pakati pawo ndi kudzipatula, akutero Ambuye. Musakhudze chodetsedwa chilichonse, ndipo ndidzakulandirani.”
18 And will be to you a Father, And ye shall be to me sons and daughters, saith the Lord Almighty.
Ndipo “Ndidzakhala Atate anu, ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi, akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”

< 2 Corinthians 6 >