+ Psalms 1 >
1 Happy are those who do not follow the counsel of the wicked, not halting in ways frequented by sinners, nor taking a seat in a gathering of scoffers.
Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2 But the law of the Lord is their joy, they study it day and night.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3 They are like trees planted by runlets of water, yielding fruit in due season, leaves never fading. In all that they do, they prosper.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4 Not so fare the wicked, not so; like chaff are they, blown by the wind.
Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5 So the wicked will not stand firm in the judgment, nor sinners appear, when the righteous are gathered.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6 For the way of the righteous is dear to the Lord, but the way of the wicked will end in ruin.
Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.