< Revelation 8 >
1 As soon as the Lamb had broken the seventh seal, there was silence in heaven for, it might be, half an hour.
Atatsekula chomatira chachisanu ndi chiwiri, kumwamba kunakhala chete mphindi makumi atatu.
2 Then I saw the seven angels who stand before God, and seven trumpets were given to them.
Ndipo ndinaona angelo asanu ndi awiri aja amene amayimirira pamaso pa Mulungu, akupatsidwa malipenga asanu ndi awiri.
3 Next, another angel came and stood at the altar with a golden censer in his hand; and a great quantity of incense was given to him, to mingle with the prayers of all Christ’s people on the golden altar before the throne.
Mngelo wina amene anali ndi chofukizira chagolide anabwera nayimirira pa guwa lansembe. Anapatsidwa lubani wambiri kuti amupereke pamodzi ndi mapemphero a anthu onse oyera mtima pa guwa lansembe lagolide patsogolo pa mpando waufumu.
4 The smoke of the incense ascended, with the prayers of Christ’s people, from the hand of the angel before God.
Fungo la lubani pamodzi ndi mapemphero a oyera mtima zinakwera kumwamba kwa Mulungu kuchokera mʼdzanja la mngeloyo.
5 Then the angel took the censer, and filled it with fire from the altar, and threw it down on the earth; and there followed peals of thunder, cries, flashes of lightning, and an earthquake.
Kenaka mngeloyo anatenga chofukizira nachidzaza ndi moto wochokera pa guwa lansembe ndi kuponya pa dziko lapansi ndipo nthawi yomweyo panachitika mabingu, phokoso, mphenzi ndi chivomerezi.
6 Then the seven angels holding the seven trumpets prepared to blow their blasts.
Angelo asanu ndi awiri anakonzekera kuyimba malipenga asanu ndi awiri.
7 The first blew; and there came hail and fire mixed with blood, and it fell on the earth. A third part of the earth was burnt up, and a third of the trees, and every blade of grass.
Mngelo woyamba anayimba lipenga lake ndipo kunabwera matalala ndi moto wosakanizana ndi magazi ndipo unaponyedwa pa dziko lapansi. Gawo limodzi la magawo atatu a dziko lapansi linapsa, gawo limodzi la magawo atatu a mitengo linapsa ndi gawo limodzi la magawo atatu a udzu wauwisi linapsanso.
8 Then the second angel blew; and what appeared to be a great mountain, burning, was hurled into the sea. A third of the sea became blood,
Mngelo wachiwiri anayimba lipenga lake, ndipo chinthu china chooneka ngati phiri lalikulu loyaka moto, chinaponyedwa mʼnyanja. Gawo limodzi la magawo atatu a nyanja linasanduka magazi.
9 and a third part of all created things that are in the sea – that is, of all living things – died, and a third of the ships was destroyed.
Gawo limodzi mwa magawo atatu a zolengedwa zonse zamoyo za mʼnyanja, linafa, ndipo gawo limodzi la sitima za pamadzi linawonongedwa.
10 Then the third angel blew; and there fell from the heavens a great star, burning like a torch. It fell on a third of the rivers and on the springs.
Mngelo wachitatu anayimba lipenga lake, ndipo nyenyezi yayikulu, yoyaka ngati muni inachoka kumwamba nigwera pa gawo limodzi la magawo atatu a mitsinje ndi pa akasupe amadzi.
11 (The star is called “Wormwood.”) A third of the water became bitter as wormwood, and so bitter was the water that many died from drinking it.
Dzina la nyenyeziyo ndi Chowawa. Gawo limodzi la magawo atatu a madzi anasanduka owawa ndipo anthu ambiri anafa chifukwa cha madzi owawawo.
12 Then the fourth angel blew; and a third of the sun and a third of the moon and a third of the stars were blasted, so that a third of them was eclipsed, and for a third part of the day there was no light, and at night it was the same.
Mngelo wachinayi anayimba lipenga lake, ndipo chimodzi cha zigawo zitatu za dzuwa, za mwezi ndi za nyenyezi zinamenyedwa kotero chimodzi mwa zitatu za zonsezi zinada. Panalibenso kuwala pa chimodzi mwa zigawo zitatu za usana, ndi chimodzimodzinso usiku.
13 And, in my vision, I heard an eagle flying in mid-heaven and crying in a loud voice – “Woe, woe, woe for all who live on the earth, at the other trumpet-blasts of the three angels who have yet to blow.”
Ndinayangʼananso ndipo ndinaona ndi kumva chiwombankhanga chimene chinkawuluka mlengalenga kwambiri chikuyankhula mofuwula kuti, “Tsoka, Tsoka! Tsoka lalikulu kwa anthu okhala mʼdziko lapansi, angelo otsala aja akangoyimba malipenga awo!”