< Psalms 37 >

1 Of David. Be not kindled to wrath at the wicked, nor envious of those who work wrong;
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 for, like grass, they will speedily wither, and fade like the green of young grass.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Trust in the Lord, and do good; remain in the land, and deal faithfully:
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 then the Lord will be your delight, he will grant you your heart’s petitions.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Commit your way to the Lord; trust in him, and he will act,
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 making clear as the light your right, and your just cause clear as the noon-day.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 In silence and patience wait on the Lord. Be not kindled to anger at those who prosper. At those who execute evil devices.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Desist from anger, abandon wrath: be not kindled to anger it leads but to evil:
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 for evildoers will be cut off, but the land will be theirs, who wait on the Lord.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Yet but a little, and the wicked vanish: look at their place: they are there no more.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 But the humble will have the land, and the rapture of peace in abundance.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 The wicked plots against the righteous, snarls like a wild animal;
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 the Lord laughs, for he sees that his day is coming.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 The wicked have drawn the sword, and bent the bow, to fell the poor, to slay those who walk uprightly;
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 but their sword will pierce their own heart, and their bows will be broken in pieces.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Better is the righteous person’s little than the wealth of many wicked.
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 For the arms of the wicked will be broken, but the Lord upholds the righteous.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 The Lord watches over the days of the blameless, their heritage will continue forever.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 They will not be shamed in the evil time, in the days of famine they will be satisfied.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 Because the wicked will perish: but the foes of the Lord, like a brand in the oven, will vanish, like smoke they will vanish.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 The wicked must borrow and cannot pay back, but the righteous is lavish and gives.
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 For those blest by the Lord inherit the land, while those whom he curses will be cut off.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 The Lord supports the steps of those with whom he is pleased.
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 Though they fall, they will not be cast headlong, for the Lord holds their hands.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Never, from youth to age, have I seen the righteous forsaken, or their children begging bread.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 They are ever lavishly lending, and their children are fountains of blessing.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Turn away from evil and do good and you will live in the land forever.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 For the Lord loves justice, he does not forsake his friends. The unrighteous will be destroyed forever, and the seed of the wicked will be cut off.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 But the land will belong to the righteous, they will live upon it forever,
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 The mouth of the righteous murmurs wisdom, and words of justice are on their tongues.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 The law of their God is in their heart, their steps are never unsteady.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 The wicked watches the righteous, and seeks to put them to death.
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 But the Lord leaves them not in their hand: at their trial they will not be held guilty.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Wait on the Lord, and observe his way: he will lift you to honour the land will be yours, you will feast your eyes on the doom of the wicked.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 I have seen the wicked exultant, lifting themselves like a cedar of Lebanon.
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 But the moment I passed, they vanished! I sought for them, but they could not be found.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Preserve your honour and practise uprightness, for such a person fares well in the end.
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 But transgressors will perish together. Cut off are the wicked forever.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 The righteous are saved by the Lord, who in time of distress is their refuge:
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 the Lord helps and rescue them, from the wicked he rescues and saves them, because they take refuge in him.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Psalms 37 >