< Mark 12 >
1 Jesus began to speak to them in parables, ‘A man once planted a vineyard, put a fence round it, dug a wine-press, built a tower, and then let it out to tenants and went abroad.
Kenaka Iye anayamba kuyankhula nawo mʼmafanizo: “Munthu wina analima munda wamphesa. Anamanga mpanda mozungulira, nakumba dzenje lofinyiramo mphesa ndipo anamanga nsanja. Anawubwereketsa munda wamphesawo kwa alimi ena napita ku dziko lina.
2 At the proper time he sent a servant to the tenants, to receive from them a share of the produce of the grape harvest;
Pa nthawi yokolola anatumiza wantchito kwa alimiwo kuti akatenge kuchokera kwa iwo zina mwa zipatso za munda wamphesa.
3 but they seized him, and beat him, and sent him away empty-handed.
Koma iwo anamugwira, namumenya ndi kumupirikitsa wopanda kanthu.
4 A second time the owner sent a servant to them; this man, too, the tenants struck on the head, and insulted.
Kenaka anatumizanso wantchito wina kwa iwo. Iwo anamumenya munthuyo pamutu ndipo anamuzunza mochititsa manyazi.
5 He sent another, but him they killed; and so with many others – some they beat and some they killed.
Anatumizanso wina, ndipo iwo anamupha. Anatumizanso ena ambiri; ena a iwo anawamenya, ena anawapha.
6 He had still one son, who was very dear to him; and him he sent to them last of all. “They will respect my son,” he said.
“Munthu uja anatsala ndi mwana mmodzi, wamwamuna amene amamukonda. Pomaliza anamutumiza mwanayo nati, ‘Adzamuchitira ulemu mwana wanga.’
7 But those tenants said to one another “Here is the heir! Come, let us kill him, and his inheritance will be ours.”
“Koma alimi aja anati kwa wina ndi mnzake, ‘Uyu ndi mlowamʼmalo. Tiyeni timuphe, ndipo cholowacho chidzakhala chathu.’
8 So they seized him, and killed him, and threw his body outside the vineyard.
Ndipo anamutenga ndi kumupha, ndipo anamuponya kunja kwa munda wamphesa.
9 What will the owner of the vineyard do? He will come and put the tenants to death, and he will let the vineyard to others.
“Kodi nanga mwini munda wamphesa adzachita chiyani? Iye adzabwera ndi kupha alimiwo nadzapereka munda wamphesawo kwa ena.
10 ‘Have you never read this passage of scripture? – “The stone which the builders despised has now itself become the cornerstone;
Kodi simunawerenge lemba lakuti: “‘Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wakhala mwala wa pa ngodya.
11 this cornerstone has come from the Lord, and is marvellous in our eyes.”’
Ambuye achita zimenezi, ndipo ndi zodabwitsa mʼmaso mwathu?’”
12 After this his enemies were eager to arrest him, but they were afraid of the crowd; for they saw that it was at them that he had aimed the parable. So they left him alone, and went away.
Ndipo akulu a ansembe, aphunzitsi a malamulo ndi akuluakulu anafunafuna njira yoti amugwirire Iye chifukwa amadziwa kuti anayankhula fanizoli mowatsutsa iwo. Koma amaopa gulu la anthu; ndipo anamusiya napita.
13 Afterwards they sent to Jesus some of the Pharisees and Herodians, to set a trap for him in the course of conversation.
Pambuyo pake anatuma ena a Afarisi ndi Aherode kwa Yesu kuti adzamukole mawu ake.
14 These men came to him and said, ‘Teacher, we know that you are an honest man, and are not afraid of anyone, for you pay no regard to a person’s position, but teach the way of God honestly; are we right in paying taxes to the Emperor, or not?
Iwo anabwera kwa Iye nati, “Aphunzitsi, ife tikudziwa kuti Inu ndi munthu amene mumanena zoona. Inu simutengeka ndi anthu, chifukwa simusamala kuti ndi ndani; koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu molingana ndi choonadi. Kodi ndi koyenera kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?
15 Should we pay, or should we not pay?’ Knowing their hypocrisy, Jesus said to them, ‘Why are you testing me? Bring me a coin to look at.’
Kodi ife tipereke msonkho kapena ayi?” Koma Yesu anadziwa chinyengo chawo. Iye anafunsa kuti, “Bwanji mukufuna kundipeza chifukwa? Bweretsani ndalama kuti ndiyione.”
16 And, when they had brought it, he asked, ‘Whose head and title are these?’ ‘The Emperor’s,’ they said;
Iwo anamubweretsera ndalama, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi nkhope iyi ndi ya ndani? Nanga malembawa ndi a ndani?” Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.”
17 and Jesus replied, ‘Pay to the Emperor what belongs to the Emperor, and to God what belongs to God.’ And they were amazed at him.
Ndipo Yesu anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.” Ndipo anazizwa naye.
18 Next came some Sadducees – the men who maintain that there is no resurrection. Their question was this –
Kenaka Asaduki, amene amati kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Iye ndi funso.
19 ‘Teacher, in our scriptures Moses decreed that, should a man’s brother die, leaving a widow but no child, the man should take the widow as his wife, and raise up a family for his brother.
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
20 There were once seven brothers. The eldest married, but died and left no family;
Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyamba anakwatira namwalira wosabereka ana.
21 and the second married his widow, and died without family; and so did the third.
Wachiwiri anakwatira mkazi wamasiyeyo, koma iye anamwalira wosabereka mwana. Zinali chimodzimodzi ndi wachitatu.
22 All the seven died and left no family. The woman herself died last of all.
Kunena zoona, palibe ndi mmodzi yemwe wa asanu ndi awiriwo anasiya ana. Pomaliza, mkaziyo anamwaliranso.
23 At the resurrection whose wife will she be, all seven brothers having had her as their wife?’
Pa kuuka kwa akufa, adzakhala mkazi wa yani pakuti anakwatiwa ndi onse asanu ndi awiri?”
24 ‘Is not the reason of your mistake,’ answered Jesus, ‘your ignorance of the scriptures and of the power of God?
Yesu anawafunsa kuti, “Kodi si pamenepa nanga pomwe mumalakwira chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu za Mulungu?
25 When people rise from the dead, there is no marrying or being married; but they are as angels in heaven.
Pamene akufa auka, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
26 ‘As to the dead, and the fact that they rise, have you never read in the book of Moses, in the passage about the Bush, how God spoke to him saying – “I am the God of Abraham, and the God of Isaac, and the God of Jacob”?
Tsopano kunena zakuti akufa amauka, kodi simunawerenge mʼbuku la Mose, pa nkhani yachitsamba choyaka moto, mmene Mulungu anati kwa iye, ‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo?’
27 He is not God of dead people, but of living. You are greatly mistaken.’
Iye si Mulungu wa anthu akufa, koma wa amoyo. Inu mwalakwitsa kwambiri!”
28 Then came up one of the teachers of the Law who had heard their discussions. Knowing that Jesus had answered them wisely, he asked him this question, ‘Which commandment is the most important of all?’
Mmodzi wa aphunzitsi amalamulo anabwera namva iwo akukambirana motsutsana. Poona kuti Yesu anawapatsa yankho labwino, anamufunsa Iye kuti, “Mwa malamulo onse, kodi lopambana koposa ndi liti?”
29 ‘The most important,’ answered Jesus, ‘is – “Hear, Israel; the Lord our God is the one Lord;
Yesu anayankha kuti, “Lamulo loposa onse ndi ili: ‘Tamvani inu Aisraeli! Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi!
30 and you must love the Lord your God with all your heart, and with all your soul, and with all your mind, and with all your strength.”
Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse ndi mphamvu zako zonse.’
31 The second is this – “You must love your neighbour as you love yourself.” There is no commandment greater than these.’
Lachiwiri ndi ili: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’ Palibe lamulo lina loposa amenewa.”
32 ‘Wisely answered, teacher!’ exclaimed the teacher of the Law. ‘It is true, as you say, that there is one God, and that there is no other besides him;
Munthuyo anayankha kuti, “Mwanena bwino Aphunzitsi. Mwalondola ponena kuti Mulungu ndi mmodzi ndipo palibe wina wofanana naye koma Iye yekha.
33 and to love him with all one’s heart, and with all one’s understanding, and with all one’s strength, and to love one’s neighbour as one loves oneself is far beyond all burnt offerings and sacrifices.’
Kumukonda Iye; ndi mtima wako wonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mphamvu zako zonse, ndi kukonda mnansi wako monga iwe mwini, ndi zopambana kuposa zopereka ndi nsembe zopsereza.”
34 Seeing that he had answered with discernment, Jesus said to him, ‘You are not far from the kingdom of God.’ After that no one ventured to question him further.
Yesu ataona kuti wayankha mwanzeru, anati kwa iye, “Iwe suli kutali ndi ufumu wa Mulungu.” Ndipo kuyambira pamenepo panalibe ndi mmodzi yemwe anayesa kumufunsanso.
35 While Jesus was teaching in the Temple Courts, he asked, ‘How is it that the teachers of the Law say that the Christ is to be David’s son?
Yesu akuphunzitsa mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amanena kuti, ‘Khristu ndi Mwana wa Davide?’
36 David said himself, speaking under the inspiration of the Holy Spirit – “The Lord said to my lord: Sit at my right hand, until I put your enemies beneath your feet.”
Pajatu Davide mwini wake, poyankhula mwa Mzimu Woyera, ananena kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani pa dzanja langa lamanja kufikira nditayika adani anu pansi pa mapazi anu.’
37 David himself calls him “lord,” how comes it, then, that he is to be his son?’ The mass of the people listened to Jesus with delight.
Davide mwini wake amutchula Iye, ‘Ambuye.’ Nanga angakhale bwanji mwana wake?” Gulu lalikulu la anthu linamvetsera ndi chisangalalo.
38 In the course of his teaching, Jesus said, ‘See that you are on your guard against the teachers of the Law, who delight to walk about in long robes, and to be greeted in the streets with respect,
Pamene ankaphunzitsa, Yesu anati, “Samalani ndi aphunzitsi a malamulo. Amakonda kuyendayenda atavala mikanjo ikuluikulu ndi kumalonjeredwa mʼmisika.
39 and to have the best seats in the synagogues, and places of honour at dinner.
Ndipo amakhala pa mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malo aulemu pa maphwando.
40 They are the men who rob widows of their homes, and make a pretence of saying long prayers. Their sentence will be all the heavier.’
Amawononga chuma cha akazi amasiye ndiponso amapemphera mapemphero aatali odzionetsera. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”
41 Then Jesus sat down opposite the chests for the Temple offerings, and watched how the people put money into them. Many rich people were putting in large sums;
Yesu anakhala pansi moyangʼanana ndi pamene amaperekera zopereka ndipo amaona anthu akupereka ndalama zawo mʼthumba la Nyumba ya Mulungu. Anthu ambiri olemera anaponya ndalama zambiri.
42 but one poor widow came and put in two small coins, worth very little.
Koma mkazi wamasiye, wosauka anabwera ndi kuyikamo tindalama tiwiri ta kopala, tongokwanira theka la ndalama.
43 Then, calling his disciples to him, Jesus said, ‘I tell you that this poor widow has put in more than all the others who were putting money into the chests;
Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mayi wosauka wamasiyeyu waponya zambiri mʼthumbali kuposa ena onsewa.
44 for everyone else put in something from what he had to spare, while she, in her need, put in all she had – everything that she had to live on.’
Iwo apereka molingana ndi chuma chawo; koma iye, mwaumphawi wake, wapereka zonse anali nazo ngakhale zoti akanagulira chakudya.”