< Exodus 12 >
1 Adonai spoke to Moses [Drawn out] and Aaron [Light-bringer] in the land of Egypt [Abode of slavery], saying,
Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti,
2 “This month shall be to you the beginning of months. It shall be the first month Nissan ·Miracles (in Aramaic), 1· of the year to you.
“Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka.
3 Speak to all the congregation of Israel [God prevails], saying, ‘On the tenth day of this month, they shall take to them every man a lamb, according to their fathers’ houses, a lamb for a household;
Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi.
4 and if the household is too little for a lamb, then he and his neighbor next to his house shall take one according to the number of the souls; according to what everyone can eat you shall make your count for the lamb.
Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere.
5 Your lamb shall be without defect, a male a year old. You shall take it from the sheep, or from the goats:
Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi.
6 and you shall keep it until the fourteenth day of the same month; and the whole assembly of the congregation of Israel [God prevails] shall kill it at evening.
Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo.
7 They shall take some of the blood, and put it on the two door posts and on the lintel, on the houses in which they shall eat it.
Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo.
8 They shall eat the meat in that night, roasted with fire, and matzah ·unleavened bread·. They shall eat it with bitter herbs.
Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa.
9 Don’t eat it raw, nor boiled at all with water, but roasted with fire; with its head, its legs and its inner parts.
Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba.
10 You shall let nothing of it remain until the morning; but that which remains of it until the morning you shall burn with fire.
Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe.
11 This is how you shall eat it: with your belt on your waist, your shoes on your feet, and your staff in your hand; and you shall eat it in haste: it is Adonai’s Pesac ·Passover·.
Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.
12 For I will go through the land of Egypt [Abode of slavery] in that night, and will strike all the firstborn in the land of Egypt [Abode of slavery], both man and animal. Against all the deities of Egypt [Abode of slavery] I will execute judgments: I am Adonai.
“Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova.
13 The blood shall be to you for a token on the houses where you are: and when I see the blood, I will pass over you, and there shall no plague be on you to destroy you, when I strike the land of Egypt [Abode of slavery].
Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.
14 This day shall be to you for a memorial, and you shall keep it a feast to Adonai: throughout all your generations you shall keep it a feast by this regulation forever.
“Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova.
15 “‘Seven days you shall eat matzah ·unleavened bread·; even the first day you shall put away yeast out of your houses, for whoever eats leavened bread from the first day until the seventh day, that soul shall be cut off from Israel [God prevails].
Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli.
16 In the first day there shall be to you a holy convocation, and in the seventh day a holy convocation; no kind of work shall be done in them, except that which every man must eat, that only may be done by you.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.
17 You shall observe the festival of Matzah ·Unleavened bread·; for in this same day have I brought your armies out of the land of Egypt [Abode of slavery]: therefore you shall observe this day throughout all your generations by this regulation forever.
“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya.
18 In the first month Nissan ·Miracles (in Aramaic), 1·, on the fourteenth day of the month at evening, you shall eat matzah ·unleavened bread·, until the twenty first day of the month at evening.
Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo.
19 There shall be no yeast found in your houses for seven days, for whoever eats that which is leavened, that soul shall be cut off from the congregation of Israel [God prevails], whether he be a foreigner, or one who is born in the land.
Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa.
20 You shall eat nothing leavened. In all your habitations you shall eat matzah ·unleavened bread·.’”
Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”
21 Then Moses [Drawn out] called for all the elders of Israel [God prevails], and said to them, “Draw out, and take lambs according to your families, and kill the Pesac ·Passover· lamb.
Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska.
22 You shall take a bunch of hyssop, and dip it in the blood that is in the basin, and strike the lintel and the two door posts with the blood that is in the basin; and none of you shall go out of the door of his house until the morning.
Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa.
23 For Adonai will pass through to strike the Egyptians [people from Abode of slavery]; and when he sees the blood on the lintel, and on the two door posts, Adonai will pass over the door, and will not allow the destroyer to come in to your houses to strike you.
Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.
24 You shall observe this thing for an statute to you and to your sons forever.
“Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu.
25 It shall happen when you have come to the land which Adonai will give you, according as he has promised, that you shall keep this service.
Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu.
26 It will happen, when your children ask you, ‘What do you mean by this service?’
Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’
27 that you shall say, ‘It is the sacrifice of Adonai’s Pesac ·Passover·, who passed over the houses of the children of Israel [God prevails] in Egypt [Abode of slavery], when he struck the Egyptians [people from Abode of slavery], and spared our houses.’” The people bowed their heads and worshiped.
Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’” Kenaka anthu anawerama napembedza.
28 The children of Israel [God prevails] went and did so; as Adonai had enjoined Moses [Drawn out] and Aaron [Light-bringer], so they did.
Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
29 At midnight, Adonai struck all the firstborn in the land of Egypt [Abode of slavery], from the firstborn of Pharaoh who sat on his throne to the firstborn of the captive who was in the dungeon; and all the firstborn of livestock.
Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo.
30 Pharaoh rose up in the night, he, and all his servants, and all the Egyptians [people from Abode of slavery]; and there was a great cry in Egypt [Abode of slavery], for there was not a house where there was not one dead.
Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.
31 He called for Moses [Drawn out] and Aaron [Light-bringer] by night, and said, “Rise up, get out from among my people, both you and the children of Israel [God prevails]; and go, abad ·serve· Adonai, as you have said!
Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha.
32 Take both your flocks and your herds, as you have said, and be gone; and bless me also!”
Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”
33 The Egyptians [people from Abode of slavery] were urgent with the people, to send them out of the land in haste, for they said, “We are all dead men.”
Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.”
34 The people took their dough before it was leavened, their kneading troughs being bound up in their clothes on their shoulders.
Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu.
35 The children of Israel [God prevails] did according to the word of Moses [Drawn out]; and they asked of the Egyptians [people from Abode of slavery] jewels of silver, and jewels of gold, and clothing.
Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala.
36 Adonai gave the people chen ·grace· in the sight of the Egyptians [people from Abode of slavery], so that they let them have what they asked. They plundered the Egyptians [people from Abode of slavery].
Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.
37 The children of Israel [God prevails] traveled from Rameses to Sukkot, about six hundred thousand on foot who were men, besides children.
Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana.
38 A mixed multitude went up also with them, with flocks, herds, and even very much livestock.
Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe.
39 They baked unleavened cakes of the dough which they brought out of Egypt [Abode of slavery]; for it was not leavened, because they were divorced out of Egypt [Abode of slavery], and couldn’t wait, and they had not prepared any food for themselves.
Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.
40 Now the time that the children of Israel [God prevails] lived in Egypt [Abode of slavery] was four hundred thirty years.
Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430.
41 At the end of four hundred thirty years, to the day, all of Adonai’s armies went out from the land of Egypt [Abode of slavery].
Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto.
42 It is a night to be much observed to Adonai for bringing them out from the land of Egypt [Abode of slavery]. This is that night of Adonai, to be much observed of all the children of Israel [God prevails] throughout their generations.
Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.
43 Adonai said to Moses [Drawn out] and Aaron [Light-bringer], “This is the regulation of the Pesac ·Passover· lamb. No foreigner shall eat of it,
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa: “Mlendo asadye Paska.
44 but every man’s servant who is bought for money, when you have circumcised him, then shall he eat of it.
Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe.
45 A foreigner and a hired servant shall not eat of it.
Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.
46 It must be eaten In one house. You shall not carry any of the meat outside of the house. Do not break any of its bones.
“Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse.
47 All the congregation of Israel [God prevails] shall keep it.
Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.
48 When a stranger shall live as a foreigner with you, and will keep the Pesac ·Passover· to Adonai, let all his males be circumcised, and then let him come near and keep it; and he shall be as one who is born in the land: but no uncircumcised person shall eat of it.
“Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska.
49 One Torah ·Teaching· shall be to him who is born at home, and to the stranger who lives as a foreigner among you.”
Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.
50 All the children of Israel [God prevails] did so. As Adonai enjoined Moses [Drawn out] and Aaron [Light-bringer], so they did.
“Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
51 That same day, Adonai brought the children of Israel [God prevails] out of the land of Egypt [Abode of slavery] by their armies.
Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”