< Zechariah 1 >

1 In the eighth month, in the second year of Darius, came the word of Jehovah to Zechariah, the son of Barachiah, the son of Iddo, the prophet, saying: —
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2 Jehovah hath been much displeased with your fathers.
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
3 But say thou to them, Thus saith Jehovah of hosts: Turn ye to me, saith Jehovah of hosts, And I will turn to you, saith Jehovah of hosts.
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Be ye not as your fathers, to whom the former prophets cried, saying, Turn ye now from your evil ways, and from your evil doings! But they did not hear, nor hearken to me, saith Jehovah.
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
5 Your fathers, where are they? And the prophets, do they live forever?
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
6 But my words and my statutes, Which I commanded my servants, the prophets, Did they not overtake your fathers? And they returned and said, Even as Jehovah of hosts thought To do to us according to our ways, and according to doings, So hath he done to us.
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
7 On the four and twentieth day of the eleventh month, which is the month Sebat, in the second year of Darius, came the word of Jehovah to Zechariah, the son of Barachiah, the son of Iddo, the prophet, saying:
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8 I saw in the night, and behold, a man riding upon a red horse; and he stood among the myrtle-trees that were in the deep valley, and behind him were other horses, red, fox-colored, and white.
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9 Then I said, What are these, my lord? And the angel that talked with me said to me, I will show thee what these are.
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10 And the man that stood among the myrtle-trees answered and said, These are they whom Jehovah hath sent to go to and fro through the earth.
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11 And they answered the angel of Jehovah that stood among the myrtle-trees, and said, We have gone to and fro through the earth, and behold, all the earth is still and at rest.
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12 Then the angel of Jehovah answered, and said, O Jehovah of hosts, how long wilt thou not have mercy on Jerusalem and the cities of Judah, against which thou hast had indignation these threescore and ten years?
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
13 And Jehovah answered the angel that talked with me good words and comfortable words.
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14 And the angel who talked with me said to me: Proclaim thou and say, Thus saith Jehovah of hosts: I am jealous for Jerusalem and for Zion with great jealousy,
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
15 And with great anger am I angry with the nations that are at ease; For I was but a little displeased, And they helped forward the affliction.
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16 Therefore thus saith Jehovah: I return to Jerusalem with mercies; My house shall be built in it, Saith Jehovah of hosts, And a measuring-line shall be stretched forth over Jerusalem.
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17 Proclaim yet and say, Thus saith Jehovah of hosts: My cities shall yet overflow with prosperity, And Jehovah will yet comfort Zion, And will yet choose Jerusalem.
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
18 Then I lifted up my eyes and looked, and behold, four horns.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
19 And I said to the angel that talked with me, What mean these? And he answered me, These are the horns which have scattered Judah, Israel, and Jerusalem.
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20 And Jehovah showed me four smiths.
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
21 Then said I, What come these to do? And he spake, saying, These are the horns which scattered Judah, so that no man lifted up his head; and now these are come to terrify them, to cast out the horns of the nations which lifted up their horn against the land of Judah to scatter it.
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”

< Zechariah 1 >