< Psalms 78 >
1 “A psalm of Asaph.” Give ear, O my people, to my instruction! Incline your ears to the words of my mouth!
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 I will open my mouth in a psalm; I will utter sayings of ancient times.
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 What we have heard and learned, And our fathers have told us,
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 We will not hide from their children; Showing to the generation to come the praises of Jehovah, His might, and the wonders he hath wrought.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 For he appointed statutes in Jacob, And established a law in Israel, Which he commanded our fathers To make known to their children;
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 So that the generation to come might know them; The children, which should be born, and rise up, Who should declare them to their children;
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 That they might put their trust in God, And not forget his deeds, But keep his commandments;
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 And might not be, like their forefathers, A stubborn and rebellious generation, —A generation whose heart was not fixed upon God, And whose spirit was not steadfast toward the Almighty.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 The children of Ephraim were like armed bowmen, Who turn their backs in the day of battle.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 They kept not the covenant of God, And refused to walk in his law;
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 And forgot his mighty deeds, And the wonders he had shown them.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Marvellous things did he in the sight of their fathers, In the land of Egypt, in the field of Zoan.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 He divided the sea, and caused them to pass through; Yea, he made the waters to stand as a heap.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 By day he led them by a cloud, And all the night by a light of fire.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 He clave the rocks in the wilderness, And gave them drink, as from the great deep.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 From the rock he brought flowing streams, And made water to run down like rivers.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Yet still they sinned against him, And provoked the Most High in the desert.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 They tempted God in their hearts, By asking food for their delight.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Yea, they spake against God, and said, “Can God spread a table in the wilderness?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Behold! he smote the rock, and the water flowed, And streams gushed forth: Is he also able to give bread? Can he provide flesh for his people?”
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 When, therefore, the LORD heard this, he was wroth: So a fire was kindled against Jacob, And anger arose against Israel.
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Because they believed not in God, And trusted not in his aid.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Yet he had commanded the clouds above, And had opened the doors of heaven;
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 And had rained down upon them manna for food, And had given them the corn of heaven.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Every one ate the food of princes; He sent them bread to the full.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Then he caused a strong wind to blow in the heavens, And by his power he brought a south wind;
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 He rained down flesh upon them as dust, And feathered fowls as the sand of the sea.
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 He caused them to fall in the midst of their camp, Round about their habitations.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 So they did eat, and were filled; For he gave them their own desire.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 Their desire was not yet satisfied, And their meat was yet in their mouths,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 When the wrath of God came upon them, And slew their strong men, And smote down the chosen men of Israel.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 For all this they sinned still, And put no trust in his wondrous works.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Therefore he consumed their days in vanity, And their years in sudden destruction.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 When he slew them, they sought him; They returned, and sought earnestly for God;
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 And remembered that God was their rock, And the Most High their redeemer.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 But they only flattered him with their mouths, And spake falsely to him with their tongues.
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 For their hearts were not true to him, Nor were they steadfast in his covenant.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Yet, being full of compassion, he forgave their iniquity, And would not utterly destroy them; Often he restrained his indignation, And stirred not up all his anger.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 He remembered that they were but flesh, —A breath, that passeth and cometh not back.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 How often did they provoke him in the wilderness! How often did they anger him in the desert!
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Again and again they tempted God, And offended the Holy One of Israel.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 They remembered not his hand, Nor the day when he delivered them from the enemy;
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 What signs he had wrought in Egypt, And what wonders in the fields of Zoan.
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 He turned their rivers into blood, So that they could not drink of their streams.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 He sent amongst them flies, which devoured them, And frogs, which destroyed them.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 He gave also their fruits to the caterpillar, And their labor to the locust.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 He destroyed their vines with hail, And their sycamore-trees with frost.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 He also gave up their cattle to hail, And their flocks to hot thunderbolts.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 He sent against them the fierceness of his anger, Wrath, indignation, and woe, —A host of angels of evil.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 He made a way for his anger, He spared them not from death, But gave up their lives to the pestilence.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 He smote all the firstborn in Egypt; The first-fruits of their strength in the tents of Ham.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 But he led forth his own people like sheep, And guided them like a flock in the wilderness.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 He led them on safely, so that they feared not, While the sea overwhelmed their enemies.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 He brought them to his own sacred border, Even to this mountain which his right hand had gained.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 He cast out the nations before them, And divided their land by a measuring-line, as an inheritance, And caused the tribes of Israel to dwell in their tents.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Yet they tempted and provoked God, the Most High, And kept not his statutes;
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Like their fathers they were faithless, and turned back; They turned aside, like a deceitful bow.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 They provoked his anger by their high places, And stirred up his jealousy by their graven images.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 God saw this, and was wroth, And greatly abhorred Israel;
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 So that he forsook the habitation at Shiloh, The tabernacle where he dwelt among men,
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 And delivered his strength into captivity, And his glory into the hand of the enemy.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 His own people he gave up to the sword, And was wroth with his own inheritance.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Fire consumed their young men, And their maidens did not bewail them.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Their priests fell by the sword, And their widows made no lamentation.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 But at length the Lord awaked as from sleep, As a hero who had been overpowered by wine;
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 He smote his enemies, and drove them back, And covered them with everlasting disgrace.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Yet he rejected the tents of Joseph, And chose not the tribe of Ephraim;
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 But chose the tribe of Judah, The Mount Zion which he loved;
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 Where he built, like the heavens, his sanctuary; Like the earth, which he hath established for ever.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 And he chose David, his servant, And took him from the sheepfolds;
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 From tending the suckling ewes he brought him To feed Jacob his people, And Israel his inheritance.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 He fed them with an upright heart, And guided them with skilful hands.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.