< Psalms 73 >

1 “BOOK III. A psalm of Asaph.” Truly God is good to Israel, —To those who are pure in heart.
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 Yet my feet almost gave way; My steps had well nigh slipped:
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 For I was envious of the proud, When I saw the prosperity of the wicked.
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 For they have no pains even to their death; Their bodies are in full health.
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 They have not the woes of other men, Neither are they smitten like other men.
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 Therefore pride encircleth their neck as a collar; Violence covereth them as a garment.
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 From their bosom issueth their iniquity; The designs of their hearts burst forth.
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 They mock, and speak of malicious oppression; Their words are haughty;
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 They stretch forth their mouth to the heavens, And their tongue goeth through the earth;
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 Therefore his people walk in their ways, And there drink from full fountains.
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 And they say, “How doth God know? How can there be knowledge with the Most High?”
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Behold these are the ungodly! Yet they are ever prosperous; they heap up riches.
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Verily I have cleansed my heart in vain; In vain have I washed my hands in innocence.
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 For every day have I been smitten; Every morn have I been chastened.
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 If I should resolve to speak like them, Surely I should be treacherous to the family of thy children.
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 So, when I studied to know this, It was painful to my eyes;
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 Until I went into the sanctuaries of God, And considered what was their end.
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Behold! thou hast set them on slippery places; Thou castest them down into unseen pits.
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 How are they brought to desolation in a moment, And utterly consumed with sudden destruction!
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 As a dream when one awaketh, Thou, O Lord! when thou awakest, wilt make their vain show a derision.
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 When my heart was vexed And I was pierced in my reins,
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 Then was I stupid and without understanding; I was like one of the brutes before thee.
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 Yet am I ever under thy care; By my right hand thou dost hold me up.
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Thou wilt guide me with thy counsel, And at last receive me in glory.
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Whom have I in heaven but thee, And whom on earth do I love in comparison with thee?
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 Though my flesh and my heart fail, God is the strength of my heart, and my portion for ever.
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 For, lo! they who are far from thee perish; Thou destroyest all who estrange themselves from thee.
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 But it is good for me to draw near to God; I put my trust in the Lord Jehovah, That I may declare all thy works.
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

< Psalms 73 >