< Psalms 63 >

1 “A psalm of David, when he was in the wilderness of Judah.” O God! thou art my God! earnestly do I seek thee! My soul thirsteth, my flesh longeth for thee, In a dry, thirsty land. where is no water!
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 Thus I look toward thee in thy sanctuary, To behold thy power and thy glory!
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 For thy loving-kindness is better than life; Therefore my lips shall praise thee!
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Thus will I bless thee, while I live; In thy name will I lift up my hands!
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 My soul shall be satisfied as with marrow and fatness, And with joyful lips my mouth shall praise thee,
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 When I think of thee upon my bed, And meditate on thee in the night-watches.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 For thou art my help, And in the shadow of thy wings I rejoice.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 My soul cleaveth to thee; Thy right hand holdeth me up.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 While they who seek to destroy my life Shall themselves go down into the depths of the earth.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 They shall be given up to the sword, And be a portion for jackals.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 But the king shall rejoice in God; All that swear by him shall be honored; But the mouth of liars shall be stopped.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< Psalms 63 >