< Psalms 145 >
1 “A song of praise. By David.” I will extol thee, my God, the King! I will praise thy name for ever and ever!
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Every day will I bless thee, And praise thy name for ever and ever!
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Great is the LORD, and greatly to be praised; Yea, his greatness is unsearchable.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 One generation shall praise thy works to another, And shall declare thy mighty deeds.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 I will speak of the glorious honor of thy majesty, And of thy wonderful works.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Men shall speak of the might of thy terrible deeds, And I will declare thy greatness;
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 They shall pour forth the praise of thy great good And sing of thy righteousness.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 The LORD is gracious, and full of compassion, Slow to anger, and rich in mercy.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 The LORD is good to all. And his tender mercies are over all his works.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 All thy works praise thee, O LORD! And thy holy ones bless thee!
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 They speak of the glory of thy kingdom, And talk of thy power;
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 To make known to the sons of men his mighty deeds, And the glorious majesty of his kingdom.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Thy kingdom is an everlasting kingdom, And thy dominion endureth throughout all generations.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 The LORD upholdeth all that fall, And raiseth up all that are bowed down.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 The eyes of all wait upon thee, And thou givest them their food in due season;
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Thou openest thine hand, And satisfiest the desire of every living thing.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 The LORD is righteous in all his ways, And merciful in all his works.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 The LORD is nigh to all that call upon him, To all that call upon him in truth.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 He fulfilleth the desire of them that fear him; He heareth their cry, and saveth them.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 The LORD preserveth all that love him; But all the wicked he will destroy.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 My mouth shall speak the praise of the LORD; And let all flesh bless his holy name for ever and ever!
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.