< Psalms 13 >

1 “For the leader of the music. A psalm of David.” How long, O LORD! wilt thou forget me for ever? How long wilt thou hide thy face from me?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2 How long shall I have anxiety in my soul for ever, And sorrow in my heart all the day? How long shall my enemy be exalted over me?
Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3 Look down and hear me, O LORD, my God! Enlighten my eyes, lest I sleep the sleep of death;
Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4 Lest my enemy say, “I have prevailed against him!” Lest my adversaries rejoice, when I am fallen.
mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5 Yet will I trust in thy goodness; My heart shall rejoice in thy salvation;
Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6 I will sing to the LORD, that he hath dealt kindly with me.
Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.

< Psalms 13 >