< Psalms 116 >

1 I rejoice that the LORD hath heard the voice of my supplication,
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 That he hath inclined his ear to me and heard me; I will call upon him as long as I live.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 The snares of death encompassed me, And the pains of the underworld seized upon me; I found distress and sorrow. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Then called I upon the LORD: O LORD! deliver me!
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Gracious is the LORD, and righteous; Yea, our God is merciful.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 The LORD preserveth the simple; I was brought low, and he helped me.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Return, O my soul! to thy rest! For the LORD hath dealt kindly with thee.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 For thou hast preserved me from death; Thou hast kept mine eyes from tears, And my feet from falling!
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 I shall walk before the LORD, In the land of the living.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 I had trust, although I said, “I am grievously afflicted!”
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 I said in my distress, “All men are liars.”
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 What shall I render to the LORD For all his benefits to me?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 I will take the cup of salvation, And call upon the name of the LORD;
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 I will pay my vows to the LORD, In the presence of all his people.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Precious in the eyes of the LORD Is the death of his holy ones.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Hear, O LORD! for I am thy servant; I am thy servant, the son of thy handmaid! Thou hast loosed my bonds.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 I will offer to thee the sacrifice of thanksgiving, And will call upon the name of the LORD.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 I will pay my vows to the LORD In the presence of all his people,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 In the courts of the house of the LORD, In the midst of thee, O Jerusalem! Praise ye the LORD!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 116 >