< Nahum 1 >
1 The prophecy concerning Nineveh. The book of the prophecy of Nahum, the Elkoshite.
Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
2 Jehovah is a jealous God, and an avenger; Jehovah is an avenger, and full of wrath! Jehovah taketh vengeance on his adversaries, And keepeth indignation for his enemies!
Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
3 Jehovah is slow to anger, but great in power; He will by no means clear the guilty; Jehovah cometh in the whirlwind and the storm, And the clouds are the dust of his feet.
Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
4 He rebuketh the sea, and maketh it dry, And drieth up all the rivers. Bashan languisheth, and Carmel, And the flower of Lebanon languisheth.
Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
5 The mountains tremble before him, And the hills melt; The earth is moved at his presence, Yea, the world and all that dwell therein.
Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
6 Who can stand before his indignation, And who can abide before the fierceness of his anger? His fury is poured out like fire, And the rocks are cast down by him!
Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
7 Jehovah is good, A stronghold in the day of trouble; He careth for them that trust in him;
Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
8 But with an overwhelming flood will he make a full end of her place, And darkness shall pursue his enemies.
koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
9 What do ye meditate against Jehovah? He will make a full end; Not the second time shall the calamity come.
Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
10 For while they are entangled like thorns, And like those that are drunk with wine, They shall be devoured as stubble fully dry.
Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11 From thee hath gone forth one that devised evil against Jehovah; That meditated destruction.
Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
12 Thus saith Jehovah: Though they be flourishing, and likewise many, Yet shall they be cut down, and pass away; I have afflicted thee, but I will afflict thee no more.
Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
13 For now will I break his yoke from off thee, And will burst thy bonds in sunder.
Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
14 And concerning thee hath Jehovah given command, That thy name shall no more be sown. From the house of thy god I will cut off the graven image and the molten image; I will make thy grave; for thou hast become vile!
Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15 Behold upon the mountains the feet of him that bringeth good tidings, That publisheth peace! Keep, O Judah, thy feasts, perform thy vows! For no more shall the destroyer pass through thee; He is utterly consumed.
Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.