< Mark 4 >
1 And again he began to teach by the shore of the lake; and there was gathered to him a very great multitude, so that he went into a boat, and sat down in it upon the lake; and all the multitude was by the lake on the land.
Nthawi inanso Yesu atakhala mʼmbali mwa nyanja, anayamba kuphunzitsa. Gulu lalikulu la anthu linasonkhana momuzungulira kotero kuti Iye analowa mʼbwato lomwe linali pa nyanja nakhalamo, anthu onse ali pa mtunda mʼmbali mwa madzi.
2 And he taught them many things in parables, and said to them in his teaching,
Anawaphunzitsa zinthu zambiri mʼmafanizo, ndipo mʼchiphunzitso chake anati:
3 Hearken: Behold, a sower went forth to sow.
“Tamverani! Mlimi anapita kukafesa mbewu zake.
4 And it came to pass, as he sowed some seeds fell by the way-side; and the birds came and devoured them.
Akufesa, mbewu zina zinagwera mʼmbali mwa njira, ndipo mbalame zinabwera ndi kuzidya.
5 And others fell on rocky ground, where they had not much earth; and they sprung up immediately, because they had no depth of earth.
Zina zinagwa pa malo a miyala pamene panalibe dothi lambiri. Zinamera mofulumira chifukwa panalibe dothi lambiri.
6 But when the sun was up, they were scorched; and because they had no root, they withered away.
Koma dzuwa litakwera, mbewuzo zinapserera, ndipo zinawuma chifukwa zinalibe mizu.
7 And others fell among thorns; and the thorns grew up, and choked them, and they yielded no fruit.
Mbewu zina zinagwa pa minga, ndipo mingayo inayanga ndi kuzirepheretsa kukula.
8 And others fell on good ground, and shooting up and growing yielded fruit; and bore as much as thirty, and sixty, and a hundred fold.
Mbewu zinanso zinagwa pa nthaka yabwino ndipo zinamera, zinakula ndi kubereka zipatso, zina zochuluka makumi atatu, zina makumi asanu ndi limodzi ndi zina 100.”
9 And he said, He that hath ears to hear, let him hear.
Pamenepo Yesu anati, “Amene ali ndi makutu akumva, amve.”
10 And when he was in private, they who were about him, with the twelve, asked him about the parables.
Ali yekha, ophunzira ndi ena omuzungulira, anamufunsa za mafanizo.
11 And he said to them, To you hath been given the mystery of the kingdom of God; but to them, who are without, all things are done in parables; t
Iye anawawuza kuti, “Chinsinsi cha ufumu wa Mulungu chapatsidwa kwa inu. Koma kwa amene ali kunja zinthu zonse zinenedwa mʼmafanizo:
12 hat seeing they may see, and not perceive, and hearing they may hear, and not understand; lest they should turn, and be forgiven.
kotero kuti, “‘Kupenya mudzapenya koma osaona kanthu, kumva mudzamva koma osamvetsetsa, kuti mwina angatembenuke ndi kukhululukidwa!’”
13 And he saith to them, Know ye not this parable? and how will ye know all the parables?
Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Kodi simukulimvetsa fanizoli? Kodi nanga mudzazindikira bwanji fanizo lina lililonse?
14 The sower soweth the word.
Wofesa amafesa mawu.
15 And these are they by the wayside, those where the word is sown, and when they have heard, Satan cometh immediately, and taketh away the word that was sown in them.
Anthu ena ali ngati mbewu za mʼmbali mwa njira, mʼmene mawu amafesedwamo. Akangowamva, Satana amabwera ndi kuchotsa mawu amene anafesedwa mwa iwo.
16 And these in like manner are they that are sown on the rocky places, those, who, when they have heard the word, immediately receive it with joy,
Ena, monga mbewu zofesedwa pa miyala, amamva mawu ndipo nthawi yomweyo amawalandira ndi chimwemwe.
17 and have no root in themselves, but endure only for a time; then, when affliction or persecution ariseth on account of the word, they immediately fall away.
Koma popeza alibe mizu, amakhala kwa kanthawi kochepa. Mavuto kapena masautso akafika chifukwa cha mawu, amagwa mofulumira.
18 And others are they that are sown among the thorns; these are they who hear the word,
Komabe ena, monga mbewu zofesedwa pakati pa minga, amamva mawu;
19 but the cares of the world, and the deceitfulness of riches, and the lusts of other things entering in, choke the word, and it becometh unfruitful. (aiōn )
koma nkhawa zamoyo uno, chinyengo cha chuma ndi zokhumba za zinthu zina zimabwera ndi kutchinga mawu, ndipo amawachititsa kukhala osabala chipatso. (aiōn )
20 And these are they who are sown on the good ground; such as hear the word, and receive it; and bear fruit, thirty, sixty, and a hundred fold.
Ena, ngati mbewu zofesedwa pa nthaka yabwino, amamva mawu, nawalandira, ndi kubereka zipatso zokwanira makumi atatu, makumi asanu ndi limodzi, kapena ngakhale 100 kuwonjezera pa zomwe zinafesedwa.”
21 And he said to them, Is a lamp brought to be put under the bushel, or under the bed, and not to be set on the lamp-stand?
Iye anawawuza kuti, “Kodi umatenga nyale ndi kuyiika pansi pa mbiya kapena pansi pa bedi? Mʼmalo mwake, kodi simuyika pa choyikapo chake?
22 For there is nothing secret, unless to be made known; nor was any thing hidden, but that it should come to light.
Pakuti chilichonse chobisika chidzayenera kuwululika, ndi chilichonse chachinsinsi chidzayenera kuonekera poyera.
23 If any one hath ears to hear, let him hear.
Ngati wina ali ndi makutu akumva, amve.”
24 And he said to them, Take heed what ye hear. With what measure ye mete, it will be measured to you, and more will be added to you.
Anapitiriza nati, “Ganizirani mosamala zimene mukumva, ndi muyeso umene mugwiritsa ntchito, mudzayesedwa nawo, ndipo ngakhale kwambiri.
25 For he that hath, to him will be given; and he that hath not, from him will be taken away even what he hath.
Amene ali nazo adzapatsidwa zochuluka; amene alibe, ngakhale zimene ali nazo zidzachotsedwa kwa iwo.”
26 And he said, Thus is the kingdom of God, as when a man has cast seed upon the ground,
Iye anatinso, “Umu ndi mmene ulili ufumu wa Mulungu. Munthu amafesa mbewu mʼnthaka.
27 and sleeps and rises night and day, and the seed springs and grows up, he knows not how.
Usiku ndi usana, kaya agona kapena adzuka, mbewu imamera ndi kukula, ngakhale sadziwa mmene zimachitikira.
28 For the earth brings forth fruit of itself, first the blade, then the ear, then the full grain in the ear.
Nthaka pa yokha imatulutsa mbewu, umayamba mʼmera, kenaka ngala, kenaka mbewu yokhwima mʼngalayo.
29 But when the fruit puts itself forth, immediately he sends out the sickle, because the harvest is come.
Mbewuyo ikangokhwima, amayimweta chifukwa nthawi yokolola yakwana.”
30 And he said, To what shall we liken the kingdom of God? or under what comparison shall we set it forth?
Ndipo anatinso, “Kodi tinene kuti ufumu wa Mulungu ufanana ndi chiyani, kapena ndi fanizo lotani limene tidzagwiritsa ntchito pakuwufotokozera?
31 It is like a grain of mustard, which, when it is sown in the earth, is less than all the seeds that are in the earth;
Uli ngati mbewu ya mpiru imene ndi mbewu yayingʼono kwambiri yomwe mumadzala mʼnthaka.
32 and when it is sown, it grows up, and becomes greater than all the herbs, and puts forth great branches, so that the birds of the air can lodge under its shade.
Koma ikadzalidwa, imakula ndi kukhala yayikulu koposa mbewu zina zonse za mʼmunda ndipo mʼnthambi zake zazikulu mbalame zamlengalenga zimadzapuma pa mthunzi wake.”
33 And with many such parables he spoke the word to them, as they were able to hear.
Ndi mafanizo ambiri onga awa Yesu anayankhula mawu kwa iwo, monga mmene akanatha kumvetsa.
34 But without a parable he did not speak to them; but in private he explained all things to his own disciples.
Iye sananene kanthu kwa iwo osagwiritsa ntchito fanizo. Koma ali yekha ndi ophunzira ake, ankawatanthauzira zonse.
35 And on the same day, when the evening was come, he saith to them, Let us pass over to the other side.
Tsiku limenelo atafika madzulo, anawuza ophunzira ake kuti, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina.”
36 And leaving the multitude, they take him with them, as he was, in the boat; and there were also other boats with him.
Atasiya gulu la anthu mʼmbuyo, anamutenga Iye, napita naye monga momwe anali mʼbwatolo. Panalinso mabwato ena pamodzi ndi Iye.
37 And there arose a great storm of wind, and the waves heat into the boat, so that it was already filling.
Mphepo yamkuntho inabuka, ndipo mafunde anawomba bwatolo, kotero kuti linali pafupi kumira.
38 And he was in the stern, asleep on the pillow; and they awake him, and say to him, Teacher, carest thou not that we are perishing?
Pa nthawi imeneyi Yesu anali akugona atatsamira pilo kumbuyo kwa bwato. Ophunzira anamudzutsa nati kwa Iye, “Aphunzitsi, kodi simukusamala kuti timira?”
39 And he arose, and rebuked the wind, and said to the waves, Peace! be still! And the wind ceased, and there was a great calm.
Yesu anauka nadzudzula mphepo nati kwa mafunde, “Chete! Khala bata!” Pamenepo mphepo inaleka ndipo kunachita bata.
40 And he said to them, Why are ye so fearful? How is it that ye have not faith?
Iye anati kwa ophunzira ake, “Muli ndi mantha chifukwa chiyani? Kodi mukanalibe chikhulupiriro?”
41 And they feared exceedingly, and said one to another, Who then is this, that even the wind and the waves obey him?
Iwo anachita mantha nafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndani? Ngakhale mphepo ndi nyanja zimumvera Iye!”