< Luke 1 >
1 Inasmuch as many have undertaken to arrange a narrative of those things which are fully believed among us,
Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
2 even as they were delivered to us by those who were eye-witnesses from the beginning and became ministers of the word,
monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
3 it seemed good to me also, having accurately traced up all things from the first, to write to thee a connected account, most excellent Theophilus,
Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
4 that thou mightst know the exact truth with regard to those things in which thou wast instructed.
kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
5 There was in the days of Herod, king of Judaea, a certain priest named Zachariah, of the course of Abijah; and he had a wife of the daughters of Aaron, and her name was Elizabeth.
Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
6 And they were both righteous in the sight of God, walking in all the commandments and ordinances of the Lord blameless.
Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
7 And they had no child, because Elizabeth was barren, and they were both far advanced in years.
Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
8 And it came to pass, that, while he was serving as priest before God in the order of his course,
Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
9 according to the custom of the priesthood the lot fell to him to go into the temple of the Lord and burn the incense.
Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
10 And the whole multitude of the people was praying without at the time of the incense.
Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
11 And there appeared to him an angel of the Lord, standing on the right of the altar of incense.
Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
12 And Zachariah was troubled at the sight, and fear fell upon him.
Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
13 But the angel said to him, Fear not, Zachariah; for thy prayer was heard, and thy wife Elizabeth shall bear thee a son; and thou shalt call his name John.
Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
14 And thou wilt have joy and gladness, and many will rejoice for his birth.
Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
15 For he will be great in the sight of the Lord; and will drink neither wine nor strong drink; and he will be filled with the Holy Spirit from his very birth.
chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
16 And many of the sons of Israel will he turn to the Lord their God.
Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
17 And he will go before his face in the spirit and power of Elijah, to turn the hearts of fathers to children, and the disobedient to the wisdom of the righteous, to make ready for the Lord a prepared people.
Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
18 And Zachariah said to the angel, Whereby shall I know this? for I am an old man, and my wife is far advanced in years.
Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
19 And the angel answering said to him, I am Gabriel, who stand in the presence of God; and I was sent to speak to thee, and to tell thee these glad tidings.
Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
20 And lo! thou shalt be silent, and not able to speak, until the day when these things shall come to pass, because thou didst not believe my words, which will be fulfilled in their season.
Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
21 And the people were looking for Zachariah, and wondering that he remained so long in the temple.
Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
22 And on coming out, he was not able to speak to them; and they perceived that he had seen a vision in the temple; and he was beckoning to them, and remained speechless.
Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
23 And it came to pass, when the days of his ministration were completed, that he returned to his house.
Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
24 And after those days his wife Elizabeth conceived, and hid herself five months, saying,
Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
25 Thus hath the Lord dealt with me in the days wherein he looked on me to take away my reproach among men.
Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
26 And in her sixth month the angel Gabriel was sent from God to a city of Galilee, called Nazareth,
Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
27 to a virgin betrothed to a man whose name was Joseph, of the house of David; and the virgin's name was Mary.
kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
28 And the angel came in to her and said, Hail, thou that art highly favored! the Lord is with thee.
Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
29 And she was troubled at the words, and was considering what this salutation could mean.
Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
30 And the angel said to her, Fear not, Mary; for thou hast found favor with God.
Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
31 And lo! thou shalt conceive in thy womb, and hear a son, and shalt call his name Jesus.
Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
32 He shall be great, and shall be called the Son of the Most High; and the Lord God will give to him the throne of David his father;
Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
33 and he shall reign over the house of Jacob for ever; and of his kingdom there shall be no end. (aiōn )
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn )
34 Then said Mary to the angel, How shall this be, since I know not a man?
Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
35 And the angel answering said to her, The Holy Spirit will come upon thee, and the power of the Most High will overshadow thee; wherefore the holy one that is to be born will be called the Son of God.
Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
36 And lo! Elizabeth, thy kinswoman, she also hath conceived a son in her old age; and this is the sixth month with her who is called barren.
Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
37 For nothing will be impossible with God.
Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
38 And Mary said, Lo, the handmaid of the Lord! May it be to me according to thy word. And the angel departed from her.
Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
39 And Mary arose and went in those days into the hill-country with haste, into a city of Judah.
Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
40 And she entered the house of Zachariah, and saluted Elizabeth.
kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
41 And it came to pass, when Elizabeth heard the salutation of Mary, that the babe leaped in her womb; and Elizabeth was filled with the Holy Spirit,
Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
42 and cried out with a loud voice, and said, Blessed art thou among women; and blessed is the fruit of thy womb!
Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
43 And whence is this to me, that the mother of my Lord should come to me?
Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
44 For lo! as soon as the voice of thy salutation came to my ears, the babe leaped in my womb in exultation.
Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
45 And blessed is she who hath believed that there will be an accomplishment of those things which were told her from the Lord.
Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
46 And Mary said, My soul magnifieth the Lord,
Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 and my spirit hath exulted in God my Saviour;
Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 for he hath looked upon the low estate of his handmaiden. For lo! from this time all generations will call me blessed;
pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 for the Mighty One hath done great things for me; and holy is his name;
pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
50 and his mercy is from generation to generation on them that fear him.
Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
51 He hath wrought mightily with his arm; he hath scattered the proud in the device of their heart.
Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 He hath cast down princes from thrones, and exalted men of low degree.
Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
53 The hungry he hath filled with good things, and the rich he hath sent away empty.
Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 He hath given help to Israel his servant, in remembrance of his mercy
Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
55 toward Abraham and his offspring for ever, as he spoke to our fathers. (aiōn )
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn )
56 And Mary abode with her about three months, and returned to her own house.
Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
57 Now Elizabeth's full time came that she should be delivered; and she brought forth a son.
Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
58 And her neighbors and her kinsfolk heard that the Lord had showed great mercy toward her; and they rejoiced with her.
Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
59 And it came to pass that on the eighth day they came to circumcise the child; and they were about to call him Zachariah, after the name of his father.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
60 And his mother answering said, Not so; but he shall be called John.
koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
61 And they said to her, There is no one of thy kindred that is called by this name.
Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
62 And they made signs to his father, how he would have him named.
Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
63 And he asked for a writing-tablet, and wrote, saying, His name is John. And they all marveled.
Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
64 And his mouth was opened immediately, and his tongue was loosed; and he spoke, blessing God.
Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
65 And fear came on all that dwelt around them; and all these things were talked of throughout the whole of the hill-country of Judaea.
Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
66 And all that heard them laid them up in their hearts, saying, What then will this child be? For the hand of the Lord was with him.
Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
67 And Zachariah his father was filled with the Holy Spirit, and prophesied, saying,
Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 Blessed be the Lord, the God of Israel! for he hath visited and redeemed his people,
“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 and hath raised up a horn of salvation for us in the house of David his servant, —
Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 as he spoke by the mouth of his holy prophets of old, (aiōn )
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn )
71 salvation from our enemies, and from the hand of all that hate us,
chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 to accomplish his mercy toward our fathers, and to remember his holy covenant,
kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 the oath which he swore to Abraham our father,
lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 to grant to us, that being delivered from the hand of our enemies, we might worship him without fear,
kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 in holiness and righteousness before him, all our days.
mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 And thou, child, shalt be called a prophet of the Most High; for thou shalt go in advance before the face of the Lord to prepare his ways,
“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 to give knowledge of salvation to his people in the remission of their sins
kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 through the tender mercy of our God, whereby the day-spring from on high hath visited us,
chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 to give light to those sitting in darkness and the shadow of death, to guide our feet into the way of peace.
kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 And the child grew, and waxed strong in spirit; and was in the deserts till the day of his manifestation to Israel.
Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.