< John 7 >
1 After these things Jesus walked in Galilee; for he would not walk in Judaea, because the Jews sought to kill him.
Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
2 Now the feast of the Jews, the feast of tabernacles, was at hand.
Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
3 His brothers therefore said to him, Depart hence, and go into Judaea, that thy disciples also may see thy works which thou art doing.
abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
4 For no one doeth anything in secret, and yet himself seeketh to be known openly. If thou doest these things, manifest thyself to the world.
Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
5 For even his brothers did not believe in him.
Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
6 Jesus saith to them, My time is not yet come; but your time is always ready.
Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
7 The world cannot hate you; but me it hateth, because I testify of it, that its works are evil.
Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
8 Go ye up to the feast; I go not up to this feast; for my time is not yet fully come.
Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
9 Having said these things, he remained in Galilee.
Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
10 But when his brothers had gone up to the feast, then he also went up, not openly, but as it were in secret.
Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
11 The Jews therefore sought him at the feast, and said, Where is that man?
Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
12 And there was much debating among the multitude concerning him. Some said, He is a good man; others said, Nay, but he deceiveth the multitude.
Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
13 No one, however, spoke openly of him, for fear of the Jews.
Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
14 But when it was now the midst of the feast, Jesus went up into the temple and taught.
Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
15 The Jews therefore marveled, saying, How knoweth this man letters, having never learned?
Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
16 Jesus therefore answered them, and said, My teaching is not mine, but his that sent me.
Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
17 If any one is desirous to do his will, he will know concerning the teaching, whether it is from God, or whether I speak from myself.
Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
18 He that speaketh from himself seeketh his own glory; but he that seeketh the glory of him that sent him, he is true, and in him is no unrighteousness.
Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
19 Hath not Moses given you the Law? and none of you keepeth the Law! Why do ye seek to kill me?
Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
20 The multitude answered, Thou hast a demon! Who seeketh to kill thee?
Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
21 Jesus answered and said to them, I have done one good work, and ye are all wondering.
Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
22 Moses hath given you circumcision, (not that it is from Moses, but from the fathers; ) and ye on the sabbath circumcise a man.
Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
23 If a man receive circumcision on the sabbath, that the law of Moses may not be broken, are ye angry at me, because I have restored soundness to the whole body of a man on the sabbath?
Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
24 Judge not according to the appearance, but judge righteous judgment.
Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
25 Then some of the men of Jerusalem said, Is not this he whom they seek to kill?
Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
26 and see! he speaketh boldly, and they say nothing to him. Have the rulers discovered certainly that this man is the Christ?
Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
27 Still, as to this man, we know whence he is; but when the Christ cometh, no one knoweth whence he is.
Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
28 Jesus therefore cried aloud, teaching in the temple and saying, Ye both know me, and ye know whence I am; and I have not come of myself, but there is in truth one who sent me, whom ye know not.
Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
29 I know him, because I am from him, and he hath sent me.
koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
30 Therefore they sought to take him; but no one laid hands on him, because his hour had not yet come.
Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
31 But of the multitude many believed in him, and said, When the Christ cometh, will he do more signs than these which this man doeth?
Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
32 The Pharisees heard the multitude thus debating concerning him; and the chief priest and the Pharisees sent officers to seize him.
Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
33 Jesus therefore said, Yet a little while I am with you, and then I go to him that sent me.
Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
34 Ye will seek me and not find me; and where I am, ye cannot come.
Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
35 The Jews therefore said among themselves, Whither will this man go, that we shall not find him? Will he go to the dispersed among the Greeks, and teach the Greeks?
Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
36 What meaneth this which he said, Ye will seek me, and not find me; and where I am, ye cannot come?
Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
37 On the last day, which is the great day, of the feast, Jesus stood and cried aloud, saying, If any one thirst, let him come to me, and drink.
Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
38 He that believeth in me, from within him, as the Scripture hath said, will flow rivers of living water.
Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
39 But this he said of the Spirit, which those that believed in him were to receive; for the Spirit was not yet, because Jesus was not yet glorified.
Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
40 Some of the multitude therefore, when they heard these words, said, This is in truth the prophet. Others said, This is the Christ.
Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
41 Others said, Doth the Christ then come from Galilee?
Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
42 Hath not the Scripture said, that the Christ cometh from the seed of David, and from Bethlehem, the town where David was?
Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
43 So there was a division among the multitude because of him.
Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
44 And some of them wished to seize him; but no one laid hands on him.
Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
45 The officers therefore came to the chief priests and Pharisees, who said to them, Why did ye not bring him?
Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
46 The officers answered, Never man spoke like this man.
Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
47 The Pharisees answered them, Have ye also been deceived?
Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
48 Hath any one of the rulers believed in him? or of the Pharisees?
“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
49 but this multitude that know not the Law are accursed.
Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
50 Nicodemus saith to them, being one of them,
Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
51 Doth our law judge a man, unless it first hear from him, and know what he doeth?
“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
52 They answered and said to him, Art thou too from Galilee? Search and see that no prophet ariseth from Galilee.
Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
53 (Joh 7:53 - 8:12: This passage is omitted as ungenuine by Tischendorf and most critical editors of the Greek Testament. It is found in some manuscripts, but not in the most ancient. It is, however, very generally regarded as a genuine relic of the teaching of Christ, though not forming a part of the fourth Gospel. I give it in the text of Tregelles, omitting the words which he incloses in brackets. Tregelles, however, does not suppose it to be genuine.) [[And they went each to his house;
Kenaka onse anachoka, napita kwawo.