< Job 9 >

1 Then Job answered and said:
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 Of a truth, I know that it is so: For how can man be just before God?
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 If he choose to contend with him, He cannot answer him to one charge of a thousand.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 He is excellent in wisdom, mighty in strength: Who hath hardened himself against him, and prospered?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 He removeth the mountains, and they know it not; He overturneth them in his anger.
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 He shaketh the earth out of her place, And the pillars thereof tremble.
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 He commandeth the sun, and it riseth not, And he sealeth up the stars.
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 He alone spreadeth out the heavens, And walketh upon the high waves of the sea.
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 He made the Bear, Orion, and the Pleiades, And the secret chambers of the South.
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 He doeth great things past finding out, Yea, wonderful things without number.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Lo! he goeth by me, but I see him not; He passeth along, but I do not perceive him.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Lo! he seizeth, and who can hinder him? Who will say to him, What doest thou?
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 God will not turn away his anger; The proud helpers are brought low before him.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 How much less shall I answer him, And choose out words to contend with him?
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Though I were innocent, I would not answer him; I would cast myself on the mercy of my judge.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Should I call, and he make answer to me, I could not believe that he listened to my voice, —
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 He who falleth upon me with a tempest, And multiplieth my wounds without cause!
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 Who will not suffer me to take my breath, But filleth me with bitterness!
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 If I look to strength, “Lo! here am I!” [[saith he, ]] If to justice, “Who shall summon me to trial?”
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Though I were upright, yet must my own mouth condemn me; Though I were innocent, He would prove me perverse.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 Though I were innocent, I would not care for myself; I would despise my life.
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 It is all one; therefore I will affirm, He destroyeth the righteous and the wicked alike.
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 When the scourge bringeth sudden destruction, He laugheth at the sufferings of the innocent.
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 The earth is given into the hands of the wicked; He covereth the face of the judges thereof; If it be not He, who is it?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 My days have been swifter than a courier; They have fled away; they have seen no good.
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 They have gone by like the reed-skiffs; Like the eagle, darting upon his prey.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 If I say, I will forget my lamentation, I will change my countenance, and take courage,
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 Still am I in dread of the multitude of my sorrows; For I know that thou wilt not hold me innocent.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 I shall be found guilty; Why then should I labor in vain?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 If I wash myself in snow, And cleanse my hands with lye,
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 Still wilt thou plunge me into the pit, So that my own clothes will abhor me.
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 For He is not a man, as I am, that I may contend with him, And that we may go together into judgment;
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 There is no umpire between us, Who may lay his hand upon us both.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Let him take from me his rod, And not dismay me with his terrors,
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Then I will speak, and not be afraid of him: For I am not so at heart.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.

< Job 9 >