< Job 8 >

1 Then answered Bildad the Shuhite, and said:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 How long wilt thou speak such things? How long shall the words of thy mouth be like a strong wind?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Will God pervert judgment? Or will the Almighty pervert justice?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 As thy children sinned against him, He hath given them up to their transgression.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 But if thou wilt seek early to God, And make thy supplication to the Almighty, —
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 If thou wilt be pure and upright, Surely he will yet arise for thee, And prosper thy righteous habitation;
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 So that thy beginning shall be small, And thy latter end very great.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 For inquire, I pray thee, of the former age, And mark what hath been searched out by their fathers;
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (For we are of yesterday and know nothing, Since our days upon the earth are but a shadow; )
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Will not they instruct thee, and tell thee, And utter words from their understanding?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 “Can the paper-reed grow up without mire? Can the bulrush grow without water?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 While it is yet in its greenness, and is not cut down, It withereth before any other herb.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Such is the fate of all who forget God; So perisheth the hope of the ungodly.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 His confidence shall come to nought, And his trust shall prove a spider's web.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 He shall lean upon his house, and it shall not stand; He shall lay fast hold on it, but it shall not endure.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 He is in full green before the sun, And his branches shoot forth over his garden;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 His roots are entwined about the heap, And he seeth the place of stones;
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 When he shall be destroyed from his place, It shall deny him, saying, 'I never saw thee.'
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Lo! such is the joy of his course! And others shall spring up from his place”
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Behold, God will not cast away an upright man; Nor will he help the evil-doers.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 While he filleth thy mouth with laughter, And thy lips with gladness,
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 They that hate thee shall be clothed with shame, And the dwelling-place of the wicked shall come to nought.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >