< Job 7 >

1 Is there not a war-service for man on the earth? Are not his days as the days of a hireling?
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 As a servant panteth for the shade, And as a hireling looketh for his wages,
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 So am I made to possess months of affliction, And wearisome nights are appointed for me.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 If I lie down, I say, When shall I arise, and the night be gone? And I am full of restlessness until the dawning of the day.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 My flesh is clothed with worms, and clods of dust; My skin is broken and become loathsome.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 My days are swifter than a weaver's shuttle; They pass away without hope.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 O remember that my life is a breath; That mine eye shall no more see good!
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 The eye of him that hath seen me shall see me no more; Thine eyes shall look for me, but I shall not be.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 As the cloud dissolveth and wasteth away, So he that goeth down to the grave shall arise no more; (Sheol h7585)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
10 No more shall he return to his house, And his dwelling-place shall know him no more.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Therefore I will not restrain my mouth; I will speak in the anguish of my spirit; I will complain in the bitterness of my soul.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Am I a sea, or a sea-monster, That thou settest a watch over me?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 When I say, My bed shall relieve me, My couch shall ease my complaint,
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 Then thou scarest me with dreams, And terrifiest me with visions;
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 So that my soul chooseth strangling, Yea, death, rather than these my bones.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 I am wasting away; I shall not live alway: Let me alone, for my days are a vapor!
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 What is man, that thou shouldst make great account him, And fix thy mind upon him?—
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 That thou shouldst visit him every morning, And prove him every moment?
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 How long ere thou wilt look away from me, And let me alone, till I have time to breathe?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 If I have sinned, what have I done to thee, O thou watcher of men! Why hast thou set me up as thy mark, So that I have become a burden to myself?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 And why dost thou not pardon my transgression, And take away mine iniquity? For soon shall I sleep in the dust; And, though thou seek me diligently, I shall not be.
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

< Job 7 >