< Job 5 >

1 Call now, see if any will answer thee! And to which of the holy ones wilt thou look?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Verily grief destroyeth the fool, And wrath consumeth the weak man.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 I have seen an impious man taking root, But soon I cursed his habitation.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 His children are far from safety; They are oppressed at the gate, and there is none to deliver them.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 His harvest the hungry devour, Carrying it even through the thorns; And a snare gapeth after his substance.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 For affliction cometh not from the dust, Nor doth trouble spring up from the ground;
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 Behold, man is born to trouble, As the sparks fly upward.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 I would look to God, And to God would I commit my cause,
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Who doeth great things and unsearchable; Yea, marvellous things without number;
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Who giveth rain upon the earth, And sendeth water upon the fields;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Who placeth the lowly in high places, And restoreth the afflicted to prosperity;
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Who disappointeth the devices of the crafty, So that their hands cannot perform their enterprises;
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Who taketh the wise in their own craftiness, And bringeth to nought the counsel of the artful.
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 They meet with darkness in the daytime; They grope at noon as if it were night.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 So he saveth the persecuted from their mouth; The oppressed from the hand of the mighty.
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 So the poor hath hope, And iniquity stoppeth her mouth.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Behold, happy is the man whom God correcteth; Therefore despise not thou the chastening of the Almighty.
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 For he bruiseth, and bindeth up; He woundeth, and his hands make whole.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 In six troubles will he deliver thee; Yea, in seven shall no evil touch thee.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 In famine he will redeem thee from death, And in war from the power of the sword.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Thou shalt be safe from the scourge of the tongue, And shalt not be afraid of destruction, when it cometh.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 At destruction and famine thou shalt laugh, And of the wild beasts of the land shalt thou not be afraid.
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 For thou shalt be in league with the stones of the field; Yea, the beasts of the forest shall be at peace with thee.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Thou shalt find that thy tent is in peace; Thou shalt visit thy dwelling, and not be disappointed.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Thou shalt see thy descendants numerous, And thine offspring as the grass of the earth.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Thou shalt come to thy grave in full age, As a shock of corn gathered in its season.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Lo! this we have searched out; so it is: Hear it, and lay it up in thy mind!
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Job 5 >