< Job 40 >

1 Moreover Jehovah spake to Job, and said:
Yehova anati kwa Yobu:
2 Will the censurer of the Almighty contend with him? Will the reprover of God answer?
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Then Job answered Jehovah, and said:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Behold, I am vile! what can I answer thee? I will lay my hand upon my mouth.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Once have I spoken, but I will not speak again; Yea, twice, but I will say no more.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Then spake Jehovah to Job out of the whirlwind, and said:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Gird up now thy loins like a man! I will ask thee, and do thou instruct me!
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Wilt thou even disannul my right? Wilt thou condemn me, that thou mayst be righteous?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Hast thou an arm like God's? Or canst thou thunder with thy voice like him?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Deck thyself with grandeur and majesty, And array thyself in splendor and glory!
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Send forth the fury of thy wrath! Look upon every proud one, and abase him!
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Look upon every proud one, and bring him low; Yea, tread down the wicked in their place!
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Hide them in the dust together; Shut up their faces in darkness!
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Then, indeed, will I give thee the praise, That thine own right hand can save thee.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Behold the river-horse, which I have made as well as thyself; He feedeth on grass like the ox.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Behold, what strength is in his loins! And what force in the muscles of his belly!
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 He bendeth his tail, like the cedar, And the sinews of his thighs are twisted together.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 His bones are pipes of brass, And his limbs are bars of iron.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 He is chief among the works of God; He that made him gave him his sword.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 For the mountains supply him with food, Where all the beasts of the field play.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 He lieth down under the lote-plants, In the covert of reeds, and in the fens.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 The lote-plants cover him with their shadow, And the willows of the brook compass him about.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Lo! the stream overfloweth, but he starteth not; He is unmoved though Jordan rush forth even to his mouth.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Can one take him before his eyes, Or pierce his nose with hooks?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Job 40 >