< Job 4 >

1 Then spake Eliphaz the Temanite, and said:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 If one attempt a word with thee, wilt thou be offended? But who can refrain from speaking?
“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
3 Behold, thou hast admonished many; Thou hast strengthened feeble hands;
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
4 Thy words have upheld him that was falling, And thou hast given strength to feeble knees.
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
5 But now it is come upon thee, and thou faintest; It toucheth thee, and thou art confounded!
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
6 Is not thy fear of God thy hope, And the uprightness of thy ways thy confidence?
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
7 Remember, I pray thee, who ever perished being innocent? Or where have the righteous been cut off?
“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
8 According to what I have seen, they who plough iniquity, And sow mischief, reap the same.
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
9 By the blast of God they perish, And by the breath of his nostrils they are consumed.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 The roaring of the lion, and the voice of the fierce lion, And the teeth of the young lions are broken.
Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 The fierce lion perisheth for lack of prey, And the whelps of the lioness are scattered abroad.
Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
12 A word was once secretly brought to me, And mine ear caught a whisper thereof.
“Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 Amid thoughts from visions of the night, When deep sleep falleth upon men,
Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 A fear and a horror came upon me, Which made all my bones to shake.
ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 Then a spirit passed before my face, The hair of my flesh rose on end;
Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 It stood still, but its form I could not discern; An image was before mine eyes; There was silence, and I heard a voice:
Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 “Shall mortal man be more just than God? Shall man be more pure than his Maker?
‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Behold, he putteth no trust in his ministering spirits, And his angels he chargeth with frailty.
Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 What then are they who dwell in houses of clay, Whose foundation is in the dust, Who crumble to pieces, as if moth-eaten!
nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 Between morning and evening are they destroyed; They perish for ever, and none regardeth it.
Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 The excellency that is in them is torn away; They die before they have become wise.”
Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

< Job 4 >