< Job 3 >
1 At length Job opened his mouth, and cursed the day of his birth.
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 And Job spake and said:
Ndipo Yobu anati:
3 Perish the day in which I was born, and the night which said, “A man-child is conceived!”
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Let that day be darkness; Let not God seek it from above; Yea, let not the light shine upon it!
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Let darkness and the shadow of death redeem it; Let a cloud dwell upon it; Let whatever darkeneth the day terrify it!
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 As for that night, let darkness seize upon it; Let it not rejoice among the days of the year; Let it not come into the number of the months!
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 O let that night be unfruitful! Let there be in it no voice of joy;
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 Let them that curse the day curse it, Who are skilful to stir up the leviathan!
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Let the stars of its twilight be darkened; Let it long for light, and have none; Neither let it see the eyelashes of the morning!
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Because it shut not up the doors of my mother's womb, And hid not trouble from mine eyes.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Why died I not at my birth? Why did I not expire when I came forth from the womb?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Why did the knees receive me, And why the breasts, that I might suck?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 For now should I lie down and be quiet; I should sleep; then should I be at rest,
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 With kings and counsellors of the earth, Who built up for themselves—ruins!
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 Or with princes that had gold, And filled their houses with silver;
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Or, as a hidden untimely birth, I had perished; As infants which never saw the light.
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 There the wicked cease from troubling; There the weary are at rest.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 There the prisoners rest together; They hear not the voice of the oppressor.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 The small and the great are there, And the servant is free from his master.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Why giveth He light to him that is in misery, And life to the bitter in soul,
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 Who long for death, and it cometh not, And dig for it more than for hid treasures;
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 Who rejoice exceedingly, Yea, exult, when they can find a grave?
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Why is light given to a man from whom the way is hid, And whom God hath hedged in?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 For my sighing cometh before I eat, And my groans are poured out like water.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 For that which I dread overtaketh me; That at which I shudder cometh upon me.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 I have no peace, nor quiet, nor respite: Misery cometh upon me continually.
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”