< Job 28 >
1 Truly there is a vein for silver, And a place for gold, which men refine.
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Iron is obtained from earth, And stone is melted into copper.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 Man putteth an end to darkness; He searcheth to the lowest depths For the stone of darkness and the shadow of death.
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 From the place where they dwell they open a shaft; Forgotten by the feet, They hang down, they swing away from men.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 The earth, out of which cometh bread, Is torn up underneath, as it were by fire.
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 Her stones are the place of sapphires, And she hath clods of gold for man.
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 The path thereto no bird knoweth, And the vulture's eye hath not seen it;
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 The fierce wild beast hath not trodden it; The lion hath not passed over it.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 Man layeth his hand upon the rock; He upturneth mountains from their roots;
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 He cleaveth out streams in the rocks, And his eye seeth every precious thing;
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 He bindeth up the streams, that they trickle not, And bringeth hidden things to light.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 But where shall wisdom be found? And where is the place of understanding?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Man knoweth not the price thereof, Nor can it be found in the land of the living.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 The deep saith, It is not in me; And the sea saith, It is not with me.
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 It cannot be gotten for gold, Nor shall silver be weighed out as the price thereof.
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 It cannot be bought with the gold of Ophir, With the precious onyx or the sapphire.
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Gold and crystal are not to be compared with it; Nor can it be purchased with jewels of fine gold.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 No mention shall be made of coral or of crystal; For wisdom is more precious than pearls.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 The topaz of Ethiopia cannot equal it, Nor can it be purchased with pure gold.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 Whence then cometh wisdom? And where is the place of understanding?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Since it is hidden from the eyes of all living, And kept close from the fowls of the air.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 Destruction and Death say, We have heard a rumor of it with our ears.
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 God knoweth the way to it; He knoweth its dwelling-place.
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 For he seeth to the ends of the earth, And surveyeth all things under the whole heaven.
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 When he gave the winds their weight, And meted out the waters by measure;
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 When he prescribed a law to the rain, And a path to the thunder-flash, —
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 Then did he see it, and make it known; He established it, and searched it out.
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 But he said unto man, Behold, the fear of the Lord, that is wisdom, And to depart from evil is understanding.
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”