< Job 27 >

1 Moreover Job continued his discourse, and said:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 As God liveth, who hath rejected my cause, And the Almighty, who hath afflicted my soul;
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 As long as my breath is in me, And the spirit of God is in my nostrils,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 Never shall my lips speak falsehood, Nor my tongue utter deceit.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 God forbid that I should acknowledge you to be just: To my last breath will I assert my integrity.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 I will hold fast my innocence, and not let it go; My heart reproacheth me for no part of my life.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 May mine enemy be as the wicked, And he that riseth up against me as the unrighteous!
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 For what is the hope of the wicked, when God cutteth off his web, And taketh away his life?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 Will he listen to his cry, When trouble cometh upon him?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Can he delight himself in the Almighty, And call at all times upon God?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 I will teach you concerning the hand of God; That which is with the Almighty I will not conceal.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 Behold, ye yourselves have all seen it; Why then do ye cherish such vain thoughts?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 This is the portion of the wicked man from God, —The inheritance which oppressors receive from the Almighty.
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 If his children be multiplied, it is for the sword; And his offspring shall not be satisfied with bread.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Those of them that escape shall be buried by Death, And their widows shall not bewail them.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Though he heap up silver as dust, And procure raiment as clay, —
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 He may procure, but the righteous shall wear it, And the innocent shall share the silver.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 He buildeth his house like the moth, Or like the shed which the watchman maketh.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 The rich man lieth down, and is not buried; In the twinkling of an eye he is no more.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Terrors pursue him like a flood; A tempest stealeth him away in the night.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 The east wind carrieth him away, and he perisheth; Yea, it sweepeth him away from his place.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 God sendeth his arrows at him, and doth not spare; He would fain escape from His hand.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 Men clap their hands at him, And hiss him away from his place.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

< Job 27 >