< Job 21 >

1 But Job answered and said:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Hear attentively my words, And let this be your consolation.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Bear with me, that I may speak; And after I have spoken, mock on!
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 Is my complaint concerning man? Why then should I not be angry?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Look upon me, and be astonished, And lay your hand upon your mouth!
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 When I think of it, I am confounded; Trembling taketh hold of my flesh.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Why is it that the wicked live, Grow old, yea, become mighty in substance?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Their children are established in their sight with them, And their offspring before their eyes.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Their houses are in peace, without fear, And the rod of God cometh not upon them.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Their bull gendereth, and faileth not; Their cow calveth, and casteth not her calf.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 They send forth their little ones like a flock, And their children dance.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 They sing to the timbrel and harp, And rejoice at the sound of the pipe.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 They spend their days in prosperity, And in a moment go down to the under-world. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 And yet they say unto God, “Depart from us! We desire not the knowledge of thy ways!
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Who is the Almighty, that we should serve him? And what will it profit us, if we pray to him?”
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 [[Ye say, ]] “Lo! their prosperity is not secure in their hands! Far from me be the conduct of the wicked!”
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 How often is it, that the lamp of the wicked is put out? And that destruction cometh upon them, And that He dispenseth to them tribulations in his anger?
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 How often are they as stubble before the wind, Or as chaff, which the whirlwind carrieth away?
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 “But” [[say ye]] “God layeth up his iniquity for his children.” Let him requite the offender, and let him feel it!
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Let his own eyes see his destruction, And let him drink of the wrath of the Almighty!
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 For what concern hath he for his household after him, When the number of his own months is completed?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Who then shall impart knowledge to God, —To him that judgeth the highest?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 One dieth in the fulness of his prosperity, Being wholly at ease and quiet;
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 His sides are full of fat, And his bones moist with marrow.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Another dieth in bitterness of soul, And hath not tasted pleasure.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Alike they lie down in the dust, And the worms cover them.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Behold, I know your thoughts, And the devices by which ye wrong me.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 For ye say, “Where is the house of the oppressor, And where the dwelling-places of the wicked?”
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Have ye never inquired of travellers, And do ye not know their tokens,
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 That the wicked is spared in the day of destruction, And that he is borne to his grave in the day of wrath?
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Who will charge him with his conduct to his face, And who will requite him for the evil he hath done?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Even this man is borne with honor to the grave; Yea, he watcheth over his tomb.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Sweet to him are the sods of the valley: And all men move after him, As multitudes without number before him.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 Why then do ye offer your vain consolations? Your answers continue false.
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Job 21 >