< Job 2 >

1 Again there was a day when the sons of God came to present themselves before Jehovah; and Satan came also among them to present himself before Jehovah.
Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
2 And Jehovah said to Satan, Whence comest thou? And Satan answered Jehovah, and said, From wandering over the earth, and walking up and down in it.
Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
3 Then said Jehovah to Satan, Hast thou observed my servant Job, that there is none like him upon the earth, an upright and good man, fearing God and departing from evil? And still he holdeth fast his integrity, although thou didst excite me against him to destroy him without a cause.
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
4 And Satan answered Jehovah, and said, Skin for skin, yea, all that a man hath will he give for his life.
Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
5 But put forth now thy hand, and touch his bone and his flesh, and to thy face will he renounce thee.
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
6 And Jehovah said to Satan, Behold, he is in thy hand; but spare his life.
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
7 Then Satan went forth from the presence of Jehovah, and smote Job with sore boils from the sole of his foot to his crown.
Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
8 And he took a potsherd to scrape himself withal, and sat down among the ashes.
Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
9 Then said his wife to him, Dost thou still retain thine integrity? Renounce God, and die.
Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
10 But he said to her, Thou talkest like one of the foolish women. What! shall we receive good at the hand of God, and shall we not receive evil? In all this, Job sinned not with his lips.
Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
11 Now three friends of Job heard of all this evil that had come upon him, and came each one from his home; Eliphaz the Temanite, and Bildad the Shuhite, and Zophar the Naamathite; for they had agreed to come to mourn with him, and to comfort him.
Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
12 And they lifted up their eyes at a distance, and knew him not; then they raised their voices and wept, and rent each one his mantle, and sprinkled dust upon their heads toward heaven.
Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
13 And they sat down with him upon the ground seven days and seven nights, and none spake a word to him; for they saw that his grief was very great.
Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.

< Job 2 >