< Job 19 >
1 But Job answered and said:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 How long will ye vex my soul, And break me in pieces with words?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 These ten times have ye reviled me; Without shame do ye stun me!
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 And be it, indeed, that I have erred, My error abideth with myself.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Since, indeed, ye magnify yourselves against me, And plead against me my reproach,
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Know then that it is God who hath brought me low; He hath encompassed me with his net.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Behold, I complain of wrong, but receive no answer; I cry aloud, but obtain no justice.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 He hath fenced up my way, so that I cannot pass, And hath set darkness in my paths.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 He hath stripped me of my glory, And taken the crown from my head.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 He hath destroyed me on every side, and I am gone! He hath torn up my hope like a tree.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 He kindleth his anger against me, And counteth me as his enemy.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 His troops advance together against me; They throw up for themselves a way to me, And encamp around my dwelling.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 My brethren he hath put far from me, And my acquaintance are wholly estranged from me.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 My kinsfolk have forsaken me, And my bosom friends have forgotten me.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 The foreigners of my house, yea, my own maid-servants, regard me as a stranger; I am an alien in their eyes.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 I call my servant, and he maketh no answer; With my own mouth do I entreat him.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 My breath is become strange to my wife, And my prayers also to my own mother's sons.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Even young children despise me; When I rise up, they speak against me.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 All my bosom friends abhor me, And they whom I loved are turned against me.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 My bones cleave to my flesh and my skin, And I have scarcely escaped with the skin of my teeth.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Have pity upon me, O ye my friends! have pity upon me; For the hand of God hath smitten me!
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Why do ye persecute me like God, And are not satisfied with my flesh?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 O that my words were now written! O that they were marked down in a scroll!
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 That with an iron pen, and with lead, They were engraven upon the rock for ever!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Yet I know that my Vindicator liveth, And will hereafter stand up on the earth;
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 And though with my skin this body be wasted away, Yet without my flesh shall I see God.
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Yea, I shall see him my friend; My eyes shall behold him, and not another: For this, my soul panteth within me.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Since ye say, “How may we persecute him, And find grounds of accusation against him?”
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Be ye afraid of the sword! For malice is a crime for the sword; That ye may know that judgment cometh.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”